Mawu a M'munsi
a Mabaibulo ena anamasulira lemba limeneli kuti “Patsani.” Koma m’Chigiriki choyambirira, mawu amene anawagwiritsa ntchito amatanthauza kuchita zinthu mopitiriza. Choncho pofuna kupereka tanthauzo lenileni la mawu amene Yesu anagwiritsa ntchito palembali, Baibulo la Dziko Latsopano linamasulira lembali kuti “khalani opatsa.”