Mawu a M'munsi
e Ndime 14: Izi zikusintha zimene tinkakhulupirira pa lemba la Mateyu 13:42. Poyamba, tinkafotokoza m’mabuku athu kuti Akhristu onyenga akhala ‘akulira ndi kukukuta mano’ kwa zaka zambiri chifukwa chakuti “ana a ufumu” akuwaulula kuti ndi “ana a woipayo.” (Mat. 13:38) Komabe Baibulo limasonyeza kuti nthawi imene anthu adzakukute mano m’pamene adzawonongedwa.—Sal. 112:10.