Mawu a M'munsi
f Ndime 16: Lemba la Danieli 12:3 limanena kuti “Anthu ozindikira [Akhristu odzozedwa] adzawala ngati kuwala kwa kuthambo.” Pamene iwo ali padziko lapansi, amawala akamagwira ntchito yolalikira. Komabe, lemba la Mateyu 13:43 limatchula nthawi imene adzawale kwambiri mu Ufumu wakumwamba. M’mbuyomu, tinkakhulupirira kuti malemba onse awiriwa akunena za ntchito yolalikira.