Mawu a M'munsi
a Zikuoneka kuti ambiri mwa anthuwa anadzakhala Akhristu. Tikutero chifukwa chakuti m’kalata imene Paulo analembera Akhristu a ku Korinto, ananena kuti anthu oposa 500 aja tsopano anali “abale.” Iye ananenanso kuti: “Ambiri a iwo akali ndi moyo mpaka lero, koma ena anagona mu imfa.” Choncho zikuoneka kuti Paulo ankadziwana ndi ena mwa Akhristu amene analipo pamene Yesu ankapereka lamulo loti ophunzira ake azilalikira.