Mawu a M'munsi
b Ngakhale kuti mtumikiyu sanatchulidwe dzina m’nkhaniyi, n’kuthekadi kuti anali Eliezere. Pa nthawi imene Abulahamu analibe mwana, ankafuna kuti cholowa chake chidzaperekedwe kwa Eliezere chifukwa anali mtumiki wake wamkulu komanso wokhulupirika.—Genesis 15:2; 24:2-4.