Mawu a M'munsi
a Anthu ambiri amaona kuti Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika ndi lolondola, lodalirika komanso losavuta kuwerenga. Baibuloli linapangidwa ndi a Mboni za Yehova ndipo likupezeka m’zilankhulo zoposa 130. Mukhoza kuchita dawunilodi Baibulo limeneli pawebusaiti ya jw.org kapena pa pulogalamu ya JW Library. Komanso ngati mungakonde, a Mboni za Yehova akhoza kukupatsani Baibuloli.