Mawu a M'munsi
a Njira zochiritsira zoonedwa ndi dokotalayo kukhala zofunikira kupulumutsa moyo kapena thanzi la mwana (kuphatikizapo kuthira mwazi) zingagwiritsiridwe ntchito mwalamulo popanda chivomerezo cha makolo kapena cha khoti kokha mkati mwa vuto lamwamsanga lofuna chisamaliro panthaŵi yomweyo. Ndithudi, thayolo liyenera kukhala m’manja mwa dokotalayo pamene adalira pa mphamvu ya lamulo limeneli la zamwadzidzidzi.