Mawu a M'munsi
b MAWU OFOTOKOZERA CHITHUNZI: M’bale anayamba kutumikira pa Beteli ali wachinyamata. Kenako anakwatira n’kumachita upainiya ndi mkazi wake. Atakhala ndi ana, iye ankawaphunzitsa kulalikira. Panopa wakalamba koma akupitirizabe kuchita zonse zomwe angathe ndipo akulalikira pogwiritsa ntchito makalata.