Mawu a M'munsi
a Nthawi zambiri tikamanena za “choonadi” timatanthauza zimene timakhulupirira kapenanso zimene timachita pa moyo wathu monga Akhristu. Kaya tangophunzira kumene choonadi kapena tinayamba kalekale, tingapindule kwambiri ngati titaganizira chifukwa chake timakonda choonadicho. Tikamachita zimenezi, tidzakhala otsimikiza mtima kuti tizisangalatsa Yehova.