Mawu a M'munsi
a Yehova watipatsa chiyembekezo chabwino kwambiri cha m’tsogolo. Chiyembekezochi chimatilimbikitsa ndipo chimatithandiza kuti tisamangoganizira mavuto omwe tikukumana nawo. Chimatipatsa mphamvu kuti tipitirizebe kukhala okhulupirika kaya tikumane ndi mayesero otani. Chingatitetezenso kuti tisamatengere mfundo zimene zingasokoneze maganizo athu. Monga mmene tiphunzirire, izi ndi zifukwa zokwanira zotichititsa kuti tipitirizebe kulimbitsa chiyembekezo chathu.