Mawu a M'munsi
b MAWU OFOTOKOZERA CHITHUNZI: Monga mmene chisoti chimatetezera mutu wa msilikali, komanso mmene nangula amathandizira ngalawa kuti isayendeyende, chiyembekezo chathu chimateteza maganizo athu ndipo chimatithandiza kukhala odekha tikakumana ndi mayesero. Mlongo akupemphera ndipo sakukayikira kuti ayankhidwa. M’bale akuganizira mmene Mulungu anakwaniritsira zimene analonjeza Abulahamu. M’bale wina akuganizira mmene Mulungu wakhala akumuthandizira.