Mawu a M'munsi
a Nkhaniyi itithandiza kuti tiziyamikira kwambiri mphatso ya moyo imene Mulungu anatipatsa. Tiona njira zimene tingatsatire kuti tikhale athanzi komanso tidziteteze pakachitika ngozi za m’chilengedwe ndiponso zimene tingachite kuti tipewe ngozi zina zoopsa. Tionanso mmene tingakonzekerere ngati titafunika thandizo lachipatala lamwamsanga.