Mawu a M'munsi
a Anthu ambiri amafunitsitsa kuphunzira choonadi chifukwa choona chikondi chenicheni pakati pathu. Komabe si ife angwiro, choncho nthawi zina zingamativute kuti tichite zinthu mwachikondi ndi Akhristu anzathu. Tiyeni tikambirane chifukwa chake chikondi chili chofunika komanso mmene tingatsanzirire Yesu pa nkhani yochita zinthu ndi anthu omwe alakwitsa zinazake.