Mawu a M'munsi
a Timasangalala kwambiri tikamawerenga za zozizwitsa zomwe Yesu anachita. Mwachitsanzo, iye analetsa mphepo yamkuntho panyanja, anachiritsa odwala komanso anaukitsa akufa. Nkhani zimenezi zinalembedwa m’Baibulo osati kuti zizingotisangalatsa koma zizitiphunzitsa. Tikamaziwerenga, timaphunziramo zinthu zimene zingachititse kuti tizikhulupirira kwambiri Yehova ndi Yesu komanso kuona makhalidwe abwino amene tiyenera kukhala nawo.