Mawu a M'munsi
b Kudziwa malire athu n’kogwirizana ndi kudzichepetsa. Timasonyeza kuti tikuzindikira malire athu podziona moyenera n’kumadziwa kuti pali zina zomwe sitingakwanitse. Timasonyeza kuti ndife odzichepetsa tikamalemekeza ena komanso kuwaona kukhala otiposa. (Afil. 2:3) Kawirikawiri, munthu amene amazindikira zomwe sangakwanitse amakhalanso wodzichepetsa.