Mawu a M'munsi
a Akhristu amafuna kuti aziopa Mulungu moyenera. Mantha amenewa angateteze mtima wathu kuti tisamachite zachiwerewere kapena kuonera zolaula. Munkhaniyi, tikambirana chaputala 9 cha buku la Miyambo, chomwe chimafotokoza bwino kusiyana pakati pa nzeru ndi kupusa pogwiritsa ntchito akazi awiri ophiphiritsa. Malangizo a m’chaputalachi angatithandize panopa komanso mpaka kalekale.