Mawu a M'munsi
a Kaya zinthu ziipe bwanji padzikoli, ndife otsimikiza kuti zikhala bwino posachedwapa. Timakhulupirira kwambiri zimenezi tikamaphunzira maulosi a m’Baibulo. Munkhaniyi, tikambirana zifukwa zimene ziyenera kutichititsa kukhulupirira maulosi. Tikambirananso mwachidule awiri mwa maulosi amene Danieli analemba komanso mmene kuwamvetsa kumatithandizira.