Mawu a M'munsi
a Nkhaniyi itithandiza kuti tikwanitse kuthamanga mpikisano wokalandira moyo. Monga anthu amene tikuthamanga nawo, pali zinthu zina zimene tiyenera kunyamula. Izi zikuphatikizapo zomwe tinalonjeza kuti tidzatumikira Yehova, udindo wathu m’banja komanso kukumana ndi zotsatirapo za zimene tasankha. Komabe tiyenera kutaya cholemera chilichonse chomwe chingatilepheretse kuti tizithamanga bwino. Kodi zimenezi zikuphatikizapo chiyani? Munkhaniyi tipeza yankho la funso limeneli.