Mawu a M'munsi
a Achinyamata, Yehova amadziwa kuti mumakumana ndi mavuto amene angachititse kuti musakhale naye pa ubwenzi. Kodi mungatani kuti muzisankha mwanzeru zinthu zomwe zingasangalatse Atate wanu wakumwamba? Munkhaniyi tikambirana zitsanzo za anyamata atatu amene anadzakhala mafumu a Yuda. Tiyeni tione zimene mungaphunzire pa zimene iwo anasankha.