Mawu a M'munsi
c MAWU OFOTOKOZERA ZITHUNZI: Zithunzi zosonyeza chifukwa chake ena sangakhale ndi mwayi womva uthenga wathu womwe ukulalikidwa padziko lonse: (1) Mayi akukhala kudera limene chipembedzo chachikulu kumeneko chimalepheretsa anthu kumva uthenga wabwino, (2) banja likukhala m’dziko limene zochitika zandale zimachititsa kuti kuphunzira za Yehova kukhale koletsedwa komanso koopsa, ndipo (3) bambo akukhala m’dera lovuta kufikako.