Mawu a M'munsi
b Kusonkhanitsa “zinthu zakumwamba” komwe Paulo anatchula pa Aefeso 1:10, n’kosiyana ndi kusonkhanitsa “osankhidwa” ake komwe Yesu anatchula pa Mateyu 24:31 ndi Maliko 13:27. Paulo ankanena za nthawi imene Yehova amasankha anthu oti akalamulire limodzi ndi Yesu powadzoza ndi mzimu wake woyera. Pomwe Yesu ankanena za nthawi imene odzozedwa omwe adzakhale adakali padzikoli adzasonkhanitsidwe kupita kumwamba pa nthawi ya chisautso chachikulu.