Mawu a M'munsi
c Popemphera, Hana ananena mawu ena ofanana ndi amene Mose analemba. N’zosakayikitsa kuti ankakhala ndi nthawi yokwanira yoganizira Malemba. (Deut. 4:35; 8:18; 32:4, 39; 1 Sam. 2:2, 6, 7) Patapita zaka zambiri, Mariya, yemwe ndi Mayi wa Yesu, anagwiritsa ntchito mawu otamanda ofanana ndi amene Hana anagwiritsa ntchito.—Luka 1:46-55.