Mawu a M'munsi
b Zimene Paulo analemba zimasonyeza kuti anali ndi vuto la maso lomwe linkachititsa kuti azivutika kulemba makalata komanso kuchita utumiki wake. (Agal. 4:15; 6:11) Kapenanso mwina Paulo ankada nkhawa chifukwa cha zimene aphunzitsi abodza ankanena zokhudza iyeyo. (2 Akor. 10:10; 11:5, 13) Kaya Paulo ankada nkhawa pa zifukwa ziti, zimenezi zinkamuvutitsa maganizo.