Mawu a M'munsi
c Nthawi zina anthu ena omwe achita tchimo ndipo akufuna kuti Mulungu awakhululukire, amadziimba mlandu kwambiri moti amaona kuti sangakwanitse kupemphera. Koma Yehova amauza anthu omwe amamva mwanjira imeneyi kuti: “Tiyeni tikambirane ndipo ine ndikuthandizani kuti mukhalenso pa ubwenzi wabwino ndi ine.” (Yesaya 1:18) Iye ndi wokonzeka kulandira aliyense amene akufunitsitsa kuti akhululukidwe.