Mawu a M'munsi
a Tyndale anagwiritsa ntchito dzina lakuti “Iehouah” pomasulira mabuku 5 oyambambirira a m’Baibulo. Patapita nthawi Chingelezi chinasintha ndipo dzina la Mulungu anayamba kulilemba mogwirizana ndi mmene anthu ankalankhulira pa nthawiyo. Mwachitsanzo, mu 1612, Henry Ainsworth anagwiritsa ntchito dzina lakuti “Iehovah” pomasulira buku lonse la Masalimo. Koma pamene ankakonzanso Baibuloli mu 1639, anagwiritsa ntchito dzina lakuti “Yehova.” Nawonso omasulira Baibulo la American Standard Version, anagwiritsa ntchito dzina lakuti “Yehova” m’malo onse amene dzina la Mulungu linkapezeka m’malemba a Chiheberi.