Mawu a M'munsi
a Pulofesa wina dzina lake Robert L. Thomas, analemba zokhudza nambala ya 144,000 imene imatchulidwa pa Chivumbulutso 7:4. Iye anati: “Nambala yotchulidwa palembali ndi ya chiwerengero chenicheni cha anthu mosiyana ndi anthu otchulidwa pa Chivumbulutso 7:9 omwe chiwerengero chawo sichikudziwika. Nambalayi ikanakhala kuti si chiwerengero chenicheni cha anthu, ndiye kuti manambala onse otchulidwa m’bukuli sakanakhalanso onena za ziwerengero zenizeni.”—Chivumbulutso 1–7: Buku Exegetical Commentary, tsamba 474.