Mawu a M'munsi
c Mosiyana ndi zimene zili mu Tora, nthawi zambiri malamulo a miyambo ya Ayuda ankaletsa akazi kuphunzira Tora. Mwachitsanzo, mu Mishnah muli mawu a Rabbi Eliezer ben Hyrcanus yemwe anati: “Aliyense wophunzitsa mwana wake wamkazi Tora, zili ngati akumuphunzitsa zolaula.” (Sota 3:4) Mu Jerusalem Talmud muli chiganizo choti: “Kuli bwino kuti mawu a mu Tora awotchedwe ndi moto kusiyana n’kuti aphunzitsidwe kwa akazi.”—Sota 3:19a.