Mawu a M'munsi
a Pa Tsiku la Mwambo Wophimba Machimo, Mulungu anauza Aisiraeli kuti: “muzidzisautsa.” (Levitiko 16:29, 31) Mawu amenewa angatanthauzenso kusala kudya. (Yesaya 58:3) Baibulo lina linamasulira mawu akuti “kudzisautsa,” kuti “musadye chilichonse posonyeza kuti mukumva chisoni chifukwa cha zolakwa zanu.”—Contemporary English Version.