Mawu a M'munsi
c Buku lina linafotokoza mmene anthu anayambira kusala kudya kwa masiku 40 pokonzekera isitala. Bukuli linati: “M’zaka za m’ma 300 C.E., anthu akamakonzekera phwando la pasika (Isitala) ankasala kudya kwa mlungu umodzi wokha, ndipo nthawi zinanso ankangosala kwa tsiku limodzi kapena awiri basi. Mawu onena za kusala kudya kwa masiku 40 amapezeka m’lamulo la nambala 5 lomwe linatuluka pamsonkhano wa akuluakulu achipembedzo wa ku Nicaea (mu 325 C.E) ngakhale kuti akatswiri ena amatsutsa zoti ankanena za kusala kudya kwa masiku 40 poyembekezera kuchita Isitala.”—New Catholic Encyclopedia, Second Edition, Volume 8, patsamba 468.