Mawu a M'munsi
a Pa nkhaniyi, buku lina lofotokoza za Baibulo limanena kuti: “Zikuoneka kuti panali patapita nthawi kuchokera pamene Yosefe [mwamuna wake wa Mariya] anamwalira ndipo Yesu ndi amene ankasamalira Mariya. Koma popeza kuti Yesu anali atatsala pang’ono kuphedwa, n’kutheka kuti ankada nkhawa za amene adzasamalire mayi akewo. . . Apa Khristu anapereka chitsanzo chabwino kwa ana kuti azisamalira makolo awo achikulire.”—The NIV Matthew Henry Commentary in One Volume, pages 428-429.