Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Chikondi cha Mpeni Kumphasa
    Galamukani!—2010 | May
    • Chikondi cha Mpeni Kumphasa

      Tiyerekezere kuti muli ndi mnzanu amene munadziwana naye kuyambira muli mwana. Iye ankakuthandizani kuchita zinthu ngati munthu wamkulu komanso kuti muzigwirizana ndi anzanu ena. Mukakhala ndi nkhawa, munkangopita kwa iye kuti akuthandizeni ndipo munafika pomudalira pa zinthu zambiri.

      Koma patapita nthawi munazindikira kuti mnzanuyo si wabwino. Iye amakukakamirani kuti muziyenda naye kulikonse, ngakhale kumalo amene simungamasuke kupita naye. Ndipo ngakhale kuti nthawi zina munkaona kuti amakuthandizani kuchita zinthu mochangamuka, iye wakuwonongerani thanzi lanu. Kuwonjezera pamenepo, iye wakhalanso akukuberani ndalama zanu.

      M’zaka zaposachedwapa, mwakhala mukuyesetsa kuti musiye kucheza naye koma iye akukukakamiranibe. Inuyo mwafika pokhala kapolo wake ndipo mumadandaula kuti zinalakwika kudziwana naye.

      FODYA ali ngati bwenzi lotereli kwa anthu ambiri amene amasuta. Mayi wina dzina lake Earline, yemwe anakhala akusuta fodya kwa zaka 50, ananena kuti: “Ndinkaona kuti kusuta fodya n’kothandiza kwambiri. Fodya anafika pokhala ngati mnzanga wapamtima ndipo nthawi zambiri ndikasowa wocheza naye ndinkangoyamba kusuta.” Koma kenako Earline anazindikira kuti fodya ndi woipa komanso woopsa kwambiri. Akanapanda kusiya, bwenzi mawu oyambirira a nkhaniyi akunena za iyeyo. Iye anasiya atadziwa kuti Mulungu sasangalala ndi anthu amene amasuta fodya, chifukwa fodya amawononga thupi limene Iye anatipatsa.—2 Akorinto 7:1.

      Bambo wina dzina lake Frank anasiya kusuta n’cholinga choti asangalatse Mulungu. Koma patangopita tsiku limodzi kuchokera pamene anasiya, anapezeka kuti akukwawa m’nyumba mwake n’kumafufuza tindudu totsalira. Frank anati: “Nditaona kuti ndafika pomakwawa pansi n’kumatoleza tindudu ta fodya, ndinadzimvera chisoni kwambiri ndipo ndinaganiza zosiyiratu kusuta fodya. Kuchokera tsiku limenelo sindinasutenso fodya.”

      Kodi n’chifukwa chiyani fodya amavuta kusiya? Akatswiri ofufuza apeza kuti zinthu zotsatirazi n’zimene zimachititsa kuti anthu azivutika kusiya kusuta fodya: (1) Fodya amamulowerera munthu ngati mmene mankhwala osokoneza bongo amachitira. (2) Mu fodya muli mankhwala otchedwa nikotini omwe amafika ku ubongo m’masekondi 7 okha kuchokera pamene munthu wasuta. (3) Munthu ukamasuta fodya thupi limazolowera monga mmene limachitira ndi kudya chakudya, kumwa, kulankhula, ndi zina zotero.

      Komabe, monga mmene zinalili ndi Earline ndiponso Frank, n’zotheka kusiya chizolowezi chimenechi. Ngati inuyo mumasuta ndipo mukufuna kusiya, nkhani yotsatirayi ikuthandizani kuti muyambe moyo watsopano.

  • Khalani Wotsimikiza
    Galamukani!—2010 | May
    • Khalani Wotsimikiza

      “Anthu amene amatsimikiza mumtima mwawo kuti sadzasutanso fodya ndi amene amasiyadi kusuta.”—Linatero buku lakuti “Stop Smoking Now!”

      NGATI mukufuna kusiya kusuta, choyamba muyenera kutsimikiza kuti mukufuna kusiyadi kusuta fodya. Kodi n’chiyani chingakuthandizeni kuchita zimenezi? Muyenera kuganizira za phindu limene mungapeze ngati mutasiya kusuta.

      Simumawononga ndalama. Kusuta ngakhale paketi imodzi patsiku, kungakuwonongereni ndalama zambiri pachaka. Gyanu, yemwe amakhala ku Nepal, anati: “Ndinadabwa kwambiri nditawerengetsa ndalama zimene ndimawononga pogula fodya.”

      Mumakhala ndi moyo wosangalala. Regina yemwe amakhala ku South Africa, anati: “Nditasiya kusuta fodya, ndinayamba kukhala ndi moyo wosangalala tsiku lililonse.” Munthu amene ankasuta fodya akasiya, amayamba kumva kukoma kwa chakudya, amakhala ndi mphamvu zambiri, ndiponso amayamba kuoneka bwino.

      Mumakhala ndi thanzi labwino. “Munthu amene poyamba ankasuta fodya akangosiya kusuta, amayamba kukhala ndi thanzi labwino kwambiri. Zimenezi zimachitikira anthu amisinkhu yonse komanso aamuna kapena aakazi.”—Linatero bungwe la U.S. Centers for Disease Control and Prevention.

      Mumachita zinthu modzidalira. “Ndinasiya kusuta chifukwa chakuti sindinkafuna kuti ndikhale kapolo wa fodya. Sindinkafuna ngakhale pang’ono kukhala kapolo wa chinthu chilichonse.”—Anatero Henning, wa ku Denmark.

      Anzanu ndi achibale anu amatetezeka ku matenda. “Utsi umene anthu osuta fodya amatulutsa umayambitsa matenda osiyanasiyana kwa anthu omwe sasuta. . . . Kafukufuku akusonyeza kuti utsi wa fodya umayambitsa matenda a khansa ya m’mapapo komanso matenda a mtima, omwe amapha anthu masauzande ambiri chaka chilichonse.”—Linatero bungwe la American Cancer Society.

      Mumasangalatsa Mlengi. Baibulo limati: “Okondedwanu, tiyeni tidziyeretse kuchotsa chilichonse choipitsa cha thupi.” (2 Akorinto 7:1) Limanenanso kuti: “Mupereke matupi anu nsembe . . . yoyera, yovomerezeka kwa Mulungu.”—Aroma 12:1.

      “Ndinasiya kusuta fodya nditangodziwa kuti Mulungu sasangalala ndi zinthu zimene zimawononga thupi.”—Anatero Sylvia, wa ku Spain.

      Komabe, nthawi zina kungokhala wotsimikiza sikokwanira. Mufunikiranso kuthandizidwa ndi anthu ena, kuphatikizapo achibale ndiponso anzanu. Koma kodi iwo angatani kuti akuthandizeni?

  • Pemphani Thandizo
    Galamukani!—2010 | May
    • Pemphani Thandizo

      “Ndipo wina akam’laka mmodziyo, awiri adzachirimika.”—Mlaliki 4:12.

      NGATI tili ndi anthu otithandiza pamene tikumenyana ndi mdani, kaya mdaniyo akhale wamphamvu bwanji, nthawi zambiri timapambana. Choncho, ngati mukufuna kugonjetsa chizolowezi chosuta fodya, mungapemphe anthu ena kuti akuthandizeni. Mungapemphe anthu a pabanja panu, anzanu, kapena anthu ena amene mukuona kuti angakuthandizeni.

      Anthu amene poyamba ankasuta fodya koma anasiya angakuthandizeni kwambiri chifukwa angamvetse vuto lanu komanso angadziwe mmene angakuthandizireni. Bambo wina wa ku Denmark, dzina lake Torben, anati: “Thandizo limene ena anandipatsa kuti ndisiye kusuta fodya linali lofunika kwambiri.” Abraham, yemwe amakhala ku India, analemba kuti: “Chikondi chimene anthu apabanja panga komanso Akhristu anzanga ankandisonyeza chinandithandiza kwambiri kuti ndisiye kusuta.” Komabe nthawi zina thandizo limene achibale ndi anzanu angapereke silingakhale lokwanira.

      Mwachitsanzo, bambo wina dzina lake Bhagwandas anati: “Ndakhala ndikusuta fodya kwa zaka 27 koma nditadziwa zimene Baibulo limanena zokhudza zizolowezi zoipa, m’pamene ndinaganiza zosiya kusuta. Ndinayesetsa kuti ndichepetse kusuta. Ndinapeza anzanga ena ocheza nawo. Ndiponso ndinapita kwa alangizi kuti andithandize. Koma palibe chinathandiza. Tsiku lina usiku ndinapemphera kwa Yehova Mulungu kuti andithandize. Ndipo kenako ndinasiya kusuta.”

      Chinthu chinanso chimene chingathandize ndi kukonzekera mavuto amene mungakumane nawo ngati mutasiya kusuta. Kodi mungakumane ndi mavuto otani? Nkhani yotsatira ifotokoza za mavuto amenewa.

      [Bokosi patsamba 5]

      KODI NDI BWINO KUGWIRITSA NTCHITO MANKHWALA?

      Masiku ano kuli makampani ambiri amene akupanga mankhwala othandiza anthu kusiya kusuta fodya ndipo akupanga ndalama zambiri. Koma musanaganize zogwiritsa ntchito mankhwala amenewa, dzifunseni mafunso otsatirawa:

      Kodi ubwino wake ndi wotani? Akuti mankhwala ambiri otere amachepetsa chibaba komanso mavuto ena amene amabwera munthu akasiya kusuta fodya. Koma anthu ena amati mankhwalawa amangothandiza munthu kwa nthawi yochepa. Choncho, ngati mukufuna kugwiritsa ntchito mankhwala amenewa muyenera kufufuza kuti mudziwe zenizeni.

      Kodi kuopsa kwake n’kotani? Mankhwala ena amachititsa anthu kusanza, kukhumudwa, komanso kukhala ndi maganizo ofuna kudzipha. Dziwani kuti mankhwala ena amakhalanso ndi nikotini amene amayambitsa matenda ena. Choncho, munthu amene amagwiritsa ntchito mankhwala amenewa, chilakolako chake chofuna kusuta fodya sichitheratu.

      Kodi njira zina zosiyira fodya ndi zotani? Pakafukufuku wina, pa anthu 100 aliwonse amene anakwanitsa kusiya kusuta fodya, 88 ananena kuti anangosiya popanda kugwiritsa ntchito mankhwala aliwonse.

  • Konzekerani Kukumana ndi Mavuto
    Galamukani!—2010 | May
    • Konzekerani Kukumana ndi Mavuto

      “Ndinaganiza zosiya kusuta n’cholinga choti ndisawononge thanzi la mwana wathu wakhanda. Choncho, ndinaika m’nyumba mwathu chikwangwani chakuti ‘Osasuta Fodya.’ Koma patangopita ola limodzi ndinali ndi chibaba champhamvu kwambiri, ndipo ndinayatsa ndudu n’kuyamba kusuta.”—Anatero Yoshimitsu, wa ku Japan.

      ZIMENE zinachitikira Yoshimitsu zikusonyeza kuti anthu amene amafuna kusiya kusuta amakumana ndi mavuto. Kafukufuku akusonyeza kuti anthu 90 pa 100 alionse amene amafuna kusiya, akangosiya kwa nthawi yochepa, amayambiranso kusuta. Komabe, ngati mukuyesetsa kuti musiye kusuta, muyenera kukonzekera kukumana ndi mavuto. Kodi mavuto ena amene mungakumane nawo ndi otani?

      Chibaba: Munthu amakhala ndi chibaba champhamvu pambuyo pa masiku angapo akangosiya kusuta, koma zimenezi zimayamba kuchepa pakangodutsa milungu iwiri. Munthu wina amene anasiya kusuta ananena kuti mkati mwa masiku amenewa “chilakolako chofuna kusuta chimasinthasintha, nthawi zina chimakhala champhamvu nthawi zina chochepa.” Ngakhale patapita zaka zambiri, nthawi zina chibaba chofuna kusuta chimafika mwadzidzidzi. Ngati zimenezi zitakuchitikirani, musapupulume. Muyenera kudikira kaye mwina mphindi zisanu kapena kuposa, kenako mungaone kuti chibabacho basi chatha.

      Mavuto ena obwera chifukwa chosiya kusuta: Koyambirira, munthu amalephera kuchita zinthu mochangamuka kapena mokhazikika ndiponso amanenepa kwambiri. Nthawi zinanso amamva kupweteka ndi kuyabwa m’thupi, sachedwa kuchita thukuta, amasokomola, ndiponso sachedwa kupsa mtima kapena kukhumudwa. Koma mavutowa amatha pakapita milungu 4 kapena 6.

      Panthawi yovuta imeneyi, pali zinthu zingapo zimene zingakuthandizeni. Mwachitsanzo:

      ● Muzigona nthawi yaitali.

      ● Muzimwa madzi ndiponso madzi azipatso ambiri. Komanso muzidya chakudya cha magulu onse.

      ● Muzichita masewera olimbitsa thupi.

      ● Muzipuma mokoka mpweya ndipo muziganizira kuti tsopano mwayamba kupuma mpweya wabwino kuyerekezera ndi umene munkapuma poyamba.

      Zinthu zoyambitsa chibaba. Muyenera kusiya kuchita zinthu kapena kuganizira zinthu zimene zimakuyambitsirani chibaba. Mwachitsanzo, mwina kale munkakonda kusuta mukamamwa mowa kapena zakumwa zina. Choncho, ngati mukufuna kusiya kusuta muyeneranso kusiya kumwa zakumwazo. M’kupita kwa nthawi mukhoza kuyambiranso kumwa.

      Akatswiri amanena kuti ngakhale mutasiya kusuta, maganizo ofuna kusuta amakhalapobe. Mwachitsanzo, Torben yemwe tamutchula koyambirira uja, anati: “Papita zaka 19 kuchokera pamene ndinasiya kusuta, komabe nthawi zina ndikamamwa khofi, maganizo ofuna kusuta amandibwerera.” Komabe dziwani kuti nthawi zambiri maganizo amenewa amachepa pakapita nthawi.

      Koma mowa ndi wosiyana ndi zakumwa zina. Panthawi yonse imene mukuyesetsa kusiya kusuta, mungachite bwino kusiya kumwa mowa komanso kupewa malo amene anthu amamwerako mowa. Anthu ambiri amene amayambiranso kusuta, amachita zimenezi chifukwa chakuti anamwa mowa. Kodi n’chiyani chimachititsa zimenezi?

      ● Mowa, ngakhale wochepa kwambiri, umachititsa kuti munthu akamasuta azimva bwino.

      ● M’malo ambiri omwera mowa, mumakhala anthu ambiri osuta fodya.

      ● Munthu akaledzera amalephera kudziletsa. N’chifukwa chake Baibulo limanena kuti: ‘Vinyo amawononga nzeru za munthu.’—Hoseya 4:11.

      Anthu ocheza nawo: Muzisankha anthu abwino ocheza nawo. Musamakonde kucheza ndi anthu amene amasuta kapena amene angakulimbikitseni kusuta. Komanso muzipewa anthu amene angamakunyozeni chifukwa chakuti mwasiya kusuta.

      Kukhumudwa kapena kukwiya: Kafukufuku wina anasonyeza kuti anthu awiri mwa anthu atatu aliwonse amene amayambiranso kusuta amachita zimenezi chifukwa chokhumudwa kapena kukwiya. Ngati zinthu zimenezi zingakuchititseni kuti mukhale ndi chibaba chofuna kusuta, muyenera kusintha zimene mukuchita n’kuyamba kuchita zinthu zina monga kumwa madzi, kutafuna chingamu, kapena kupita kokayenda. Muziyesetsa kuganizira zinthu zabwino zokhazokha. Mungapemphere kwa Mulungu kapena kuwerenga Baibulo.—Salmo 19:14.

      Musamapeze Zifukwa Zodzikhululukira.

      ● Ndingosuta kamodzi kokha.

      Zoona zake: Ngakhale kusuta kamodzi kokha kungachititse kuti fodya akhale mu ubongo wanu kwa maola atatu. Ndipo zimenezi zingakuchititseni kuti musute kangapo.

      ● Kusuta kumandithandiza kwambiri ndikakhumudwa.

      Zoona zake: Kafukufuku akusonyeza kuti fodya amachititsa kuti munthu asamachedwe kukhumudwa. Anthu amene asiya kusuta fodya, koyambirira angamakhumudwe koma m’kupita kwa nthawi vutoli limatha. Choncho, ngati munthu amene wangosiya kumene kusuta atayambiranso kusuta, angamaone kuti fodya akumuthandiza kuti asamakhumudwe.

      ● Posiya kusuta panadutsa.

      Zoona zake: Maganizo akuti simungathe kusiya kusuta ndi ofoola. Baibulo limati: “Ukalefuka tsiku la tsoka mphamvu yako ichepa.” (Miyambo 24:10) Choncho, pewani maganizo akuti ndinu munthu wolephera. Munthu aliyense amene akufunadi kusiya kusuta ndipo amatsatira mfundo zothandiza ngati zimene tafotokoza m’magazini ino, angakwanitse kusiya.

      ● Sindingathe kupirira mavuto amene angabwere chifukwa chosiya kusuta.

      Zoona zake: N’zoona kuti kusiya kusuta kungabweretse mavuto aakulu, koma pakangopita milungu ingapo akhoza kuchepa. Choncho, muyenera kulimba mtima. Ngati chibaba cha fodya chitabweranso patapita miyezi kapena zaka zingapo, sichingachedwe kutha ngati inuyo mutatsimikiza kuti musasute.

      ● Ndili ndi matenda ovutika maganizo.

      Zoona zake: Ngati muli ndi matenda ovutika maganizo, muyenera kupempha dokotala wanu kuti akuthandizeni kusiya kusuta. Ngati atadziwa kuti mwasiya kusuta, iye angaone mmene angakuthandizireni, mwina angasinthe mankhwala amene akukupatsani.

      ● Ndikayambiranso kusuta, ndimaona kuti ndine wokanika.

      Zoona zake: Anthu ena amayambiranso pambuyo posiya kusuta, choncho mukayambiranso musaganize kuti ndinu wokanika. Munthu akagwa sizitanthauza kuti ali ndi vuto. Koma ngati atagwa n’kungokhala pansi pomwepo osadzuka, tingati munthuyo ali ndi vuto. Ngati mutayesetsabe, m’kupita kwa nthawi mudzakwanitsa kusiya kusuta.

      Taganizirani zimene zinachitikira Romualdo, yemwe anakhala akusuta fodya kwa zaka 26 ndipo anasiya kusuta zaka 30 zapitazo. Iye analemba kuti: “Ndikasiya kusuta, nthawi zambiri ndinkayambiranso. Ndipo ndinachita zimenezi kambirimbiri. Nthawi iliyonse imene ndasuta, ndinkaona kuti ndataika. Komabe, kenako ndinatsimikiza zokhala paubwenzi ndi Yehova Mulungu ndipo ndinkamupempha mobwerezabwereza kuti andithandize. Pamapeto pake ndinasiyiratu kusuta.”

      Nkhani yotsatira ifotokoza zinthu zinanso zimene mungachite kuti musiye kusuta n’kukhala ndi moyo wosangalala.

      [Bokosi/Chithunzi patsamba 7]

      FODYA AMAPHA

      Fodya amagwiritsidwa ntchito m’njira zambiri. Nthawi zina amaikidwa m’zakudya kapena m’mankhwala azisamba. Komabe, Bungwe Loona za Umoyo Padziko Lonse linanena kuti “kaya waikidwa mu chiyani, fodya amapha.” Izi zili choncho chifukwa chakuti fodya amayambitsa matenda oopsa monga khansa ndiponso matenda a mtima. Ngakhale amayi oyembekezera omwe amasuta amatha kuvulaza mwana wawo wosabadwa. Anthu amakonda fodya wa wamitundu yotsatirayi:

      Tindudu ting’onoting’ono topichira pamanja, tomwe n’tofala kwambiri ku mayiko a ku Asia. Tindudu timeneti n’toopsa kwambiri chifukwa timatulutsa phula, nikotini, komanso mpweya woipa wambiri kuposa fodya wamba.

      Fodya wopichiridwa patsamba la fodya kapena papepala lopangidwa kuchokeranso ku fodya. Ndudu zimenezi zikangoikidwa pakamwa, ngakhale zisanayatsidwe, fodyayo amalowerera m’thupi.

      Fodya wosakaniza ndi timbewu tinatake tonunkhira. Fodya wotereyu amatulutsa phula, nikotini, komanso mpweya wakupha wambiri kuposa fodya wamba.

      Kaliwo. Ena amaganiza kuti kugwiritsa ntchito kaliwo posuta fodya n’kosaopsa. Koma anthu amene amachita zimenezi, amatha kudwala khansa ndi matenda ena.

      Fodya wosatulutsa utsi. M’gulu limeneli muli fodya wochita kutafuna, kufwenkha ndiponso fodya winawake yemwe ndi wofala kum’mwera chakum’mawa kwa Asia wotchedwa gutkha. Mankhwala oipa a mu fodya ameneyu amalowa m’thupi kudzera mkamwa. Fodya wosatulutsa utsi ndi woopsa mofanana ndi fodya wina aliyense.

      Ena amagwiritsa ntchito chipangizo chimene chimachititsa kuti utsi wa fodya uzidutsa m’madzi, asanaumeze. Komabe, zimenezi sizichepetsa matenda amene amayambitsidwa ndi fodya monga khansa ndi matenda ena a m’mapapu.

      [Bokosi/Chithunzi patsamba 8]

      MUNGATHANDIZE BWANJI MUNTHU WINA KUSIYA KUSUTA FODYA?

      ● Muzimulimbikitsa. Kulimbikitsa ndiponso kuyamikira munthu amene akuyesetsa kusiya kusuta n’kofunika kwambiri kuposa kumangomudzudzula komanso kum’patsa malangizo. Ndi bwino kunena kuti, “Ndikuganiza kuti mutayesanso mukwanitsa,” m’malo monena kuti “Mwalepheranso?”

      ● Muzikhululuka. Munthu amene akuyesetsa kuti asiye kusuta akachita zinthu zosonyeza kuti wakwiya kapena wakhumudwa nanu, muzimukhululukira. Muzilankhula naye mokoma mtima. Mwachitsanzo, munganene kuti, “Ndikudziwa kuti n’zovuta, koma ndikusangalala kuti mumayesetsa.” Pewani kunena kuti, “Panopa ndiye mwawonjeza, ndipo zinaliko bwino panthawi yomwe munkasuta.”

      ● Muzimukonda nthawi zonse. Baibulo limati: “Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo m’bale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.” (Miyambo 17:17) Choncho, muziyesetsa kuchita zinthu moleza mtima ndiponso mwachikondi “nthawi zonse” ndi munthu amene akufuna kusiya kusuta fodya, kaya munthuyo akuchita zotani panthawiyo.

  • N’zotheka Kusiya Fodya
    Galamukani!—2010 | May
    • N’zotheka Kusiya Fodya

      TINENE kuti tsopano ‘mwalimba mtima’ kuti musiye kusuta fodya, kodi ndi mfundo ziti zomwe mungatsatire kuti zimenezo zitheke?—1 Mbiri 28:10.

      Sankhani tsiku. Dipatimenti ya zaumoyo ku United States inanena kuti munthu akaganiza zosiya kusuta, ayenera kuonetsetsa kuti waziikira malire osiya kusuta mkati mwa milungu iwiri. Kuchita zimenezi kungakuthandizeni kuti musasinthe maganizo. Lembani tsiku lomwe mwasankhalo pakalendala, dziwitsani anzanu ndipo tsikulo likafika musalisinthe, zivute zitani.

      Muziyenda ndi pepala lolembedwa kuti “Ndasiya kusuta.” Papepalapo mungalembe zinthu zomwe zingakuthandizeni kutsatira zomwe mwasankha monga:

      ● Zifukwa zosiyira.

      ● Manambala a foni a anthu amene mungawaimbire panthawi yomwe chibaba cha fodya chakubwererani.

      ● Mfundo za m’Baibulo zimene zingakuthandizeni, ngati zomwe zili pa Agalatiya 5:22, 23.

      Nthawi zonse muziyenda ndi pepala limene mwalemba kuti “Ndasiya kusuta” kuti lizikukumbutsani zomwe mwasankhazo. Ngakhale mutafika poti mwasiya kusuta, muziyenda nalobe kuti muziliwerenga mukaona kuti chibaba choti musute chayambiranso.

      Siyani zinthu zina zimene mumakonda kuchita. Tsiku lomwe mwasankha kusiya kusuta lisanafike, muyenera kusiya kaye zizolowezi zina zimene mumachita. Mwachitsanzo, ngati muli ndi chizolowezi chosuta mukangodzuka m’mawa, yesani kusintha kuti muzitha ola limodzi musanasute. Ngati mumasuta panthawi ya chakudya kapena mukangomaliza kudya, siyani kusuta panthawi imeneyi. Pewani malo amene anthu amakonda kusutirako fodya. Ndipo mukakhala nokha muziyesa kunena mokuwa kuti: “Pepani, ndasiya kusuta.” Zimenezi zingakuthandizeni kwambiri kuti musadzavutike kusiya tsiku limene mwasankha kusiya kusuta likafika. Komanso zimenezi zingakuthandizeni kuona kuti kusuta fodya ikhala mbiri yakale kwa inu.

      Konzekani. Tsiku limene mwasankha kuti musiye kusuta likayandikira, pezani zinthu zomwe mungamadye, m’malo mosuta. Mwachitsanzo, mungagule kaloti, chingamu, mtedza ndi zina zotero. Kumbutsani anzanu komanso anthu am’banja lanu za tsiku limene mukufuna kusiya komanso mmene angakuthandizireni. Tsikulo lisanafike, muyenera kutaya zotsalira zonse za fodya, machesi ndi zina zimene zingakukopeni kuti muyambirenso kusuta. Mwachitsanzo, muyenera kutaya ndudu zimene zili m’nyumba, m’galimoto, m’matumba a zovala kapena ku ofesi. Kunena zoona, n’zovuta kwambiri kupempha mnzanu kuti akupatseni fodya kapena kugula paketi ya fodya kusiyana ndi kungopita m’nyumba n’kutenga. Ndiponso, pitirizani kupempha Mulungu kuti akuthandizeni, ndipo muyenera kuyesetsa kwambiri kuchita zimenezi pamene mwasiya kusuta.—Luka 11:13.

      Anthu ambiri akwanitsa kusiya kusuta, ndipo inunso mungakwanitse. Dziwani kuti fodya ndi woipa. Kusiya kusuta kungakuthandizeni kukhala ndi thanzi labwino ndiponso kukhala wosangalala kwambiri.

      [Chithunzi patsamba 9]

      Nthawi zonse muziyenda ndi pepala limene mwalemba kuti, “Ndasiya kusuta” kuti lizikukumbutsani zomwe mwasankhazo

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena