-
Kodi Moyo Unayamba Bwanji?Galamukani!—2015 | January
-
-
NKHANI YA PACHIKUTO
Kodi Moyo Unayamba Bwanji?
Pa ziganizo zili kumanjazi,
NDI CHITI CHOMWE MUKUONA KUTI NDI CHOLONDOLA?
ZAMOYO ZINACHITA KUSINTHA KUCHOKERA KU ZINTHU ZINA
ZAMOYO ZINACHITA KULENGEDWA
ANTHU ena angaganize kuti asayansi anganene kuti chiganizo cholondola ndi choyambacho, pomwe anthu amene amakhulupirira kuti kuli Mulungu angati cholondola ndi chachiwiricho.
Komatu si asayansi onse omwe amakhulupirira kuti zamoyo zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina.
Mfundo ndi yakuti pali anthu ambiri ophunzira kuphatikizapo a sayansi ambiri omwe amakayikira zoti zamoyo zinachita kusitha kuchokera ku zinthu zina.
Wasayansi wina dzina lake Gerard, yemwe anaphunzira zoti zinthu zamoyo zinasintha kuchokera ku zinthu zina, anati: “Polemba mayeso, ndinkalemba zoti zamoyo zinachokera ku zinthu zina. Koma sikuti ndinkazikhulupirira. Ndinkangolemba zimenezi n’cholinga choti ndikhoze.”
Koma kodi n’chifukwa chiyani asayansi ena zimawavuta kukhulupirira kuti zamoyo zinachokera ku zinthu zina? Kuti tiyankhe funsoli, choyamba tiyeni tikambirane mafunso amene amazunguza mutu akatswiri akachita kafukufuku pa nkhaniyi. Mafunso ake ndi awa: (1) Kodi moyo unayamba bwanji? (2) Kodi mitundu yosiyanasiyana ya zamoyo inachokera kuti?
-
-
Mafunso Awiri Omwe Tiyenera Kudziwa Mayankho AkeGalamukani!—2015 | January
-
-
PACHIKUTO | KODI MOYO UNAYAMBA BWANJI?
Mafunso Awiri Omwe Tiyenera Kudziwa Mayankho Ake
1 Kodi Moyo Unayamba Bwanji?
ZIMENE ANTHU AMANENA: Zinthu zamoyo zinachokera ku zinthu zopanda moyo.
N’CHIFUKWA CHIYANI ANTHU ENA SAKHULUPIRIRA ZIMENEZI? Panopa asayansi amadziwa zambiri zokhudza mmene zinthu zamoyo zimapangidwira, koma amalephera kumvetsa mmene chinthu chopanda moyo chingasinthire n’kukhala chamoyo. Komanso pali kusiyana kwakukulu pakati pa zamoyo ndi zopanda moyo.
Akatswiri asayansi sadziwa bwino mmene zinthu padzikoli zinalili zaka mabiliyoni apitawo. Ndipo amasiyana maganizo pa nkhani ya kumene moyo unayambira. Ena amaganiza kuti unayambira pa chiphalaphala chochokera pansi pa nthaka. Pomwe ena amaganiza kuti unayambira pansi pa nyanja. Enanso amakhulupirira kuti moyo unayambira m’mlengalenga ndipo unafika padzikoli kudzera m’miyala yomwe inagwa kuchokera m’mlengalengamo. Koma zimenezi sizikuyankha funso lakuti moyo unayamba bwanji. Zikungosonyeza malo amene asayansi amaganiza kuti moyo unayambira.
Asayansiwa amaganiza kuti panali tizinthu tinatake totchedwa mamolekyu tokhala ndi malangizo okhudza mmene chinthu chiyenera kuonekera tomwe tinasintha n’kukhala mamolekyu amene tikuwadziwa masiku ano. Amakhulupirira kuti kenako mamolekyuwa omwe anali a zinthu zopanda moyo ankatha kusintha komanso kuchulukana. Komabe asayansi amalephera kupeza umboni woti mamolekyuwa analipodi ndipo ayeserapo kupanga mamolekyu ngati amenewa koma alephera.
Zamoyo n’zosiyana kwambiri ndi zopanda moyo chifukwa zili ndi maselo omwe amatha kusunga ndi kugwiritsa ntchito malangizo. Maselo amatha kusamutsa, kutanthauzira komanso kusunga malangizo okhudza mmene chinthu chiyenera kuonekera. Asayansi ena amaona kuti malangizowa ali ngati pulogalamu ya pakompyuta ndipo maselo ali ngati kompyutayo. Koma amene amakhulupirira kuti zinthu zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina, amalephera kufotokoza kuti malangizowa amachokera kuti.
Kuti selo lizigwira bwino ntchito limafunika mamolekyu okhala ndi mapuloteni. Puloteni iliyonse imakhala ndi tizinthu tinanso ndipo tizinthu timeneti timasanjidwa mogometsa kwambiri. Zimenezi zimapangitsa kuti puloteniyo izigwira bwino ntchito. Poona zonsezi asayansi ena amaona kuti sizingangochitika zokha kuti puloteni ipangidwe mogometsa chonchi. Wasayansi wina, dzina lake Paul Davies anati: “Poganizira mmene selo lilili komanso mmene limagwirira ntchito, zingakhale zosamveka kuganiza kuti zimenezi zinangochitika zokha.”
MFUNDO YAKE: Pambuyo pofufuza kwa zaka zambiri, asayansi alephera kupeza umboni woti zamoyo zinachokera ku zinthu zopanda moyo.
2 Kodi Mitundu Yosiyanasiyana ya Zamoyo Inachokera Kuti?
ZIMENE ANTHU AMANENA: Chinthu chamoyo choyambirira chinayamba kusintha pang’onopang’ono n’kukhala zamoyo zosiyanasiyana kuphatikizapo anthufe. Ndipo zimenezi zinkachitika potengera nyengo komanso mmene zinthu zinalili pamalowo.
N’CHIFUKWA CHIYANI ANTHU ENA SAKHULUPIRIRA ZIMENEZI? Chinthu chilichonse chamoyo chimakhala ndi maselo wamba komanso maselo ena ogometsa kwambiri. Anthu amene amakhulupirira zoti zamoyo zinachokera ku zinthu zina amati maselo wamba amatha kusintha n’kukhala maselo ogometsa kwambiri. Pa mfundoyi, buku lina linanena kuti zoti selo wamba lingasinthe n’kukhala selo logometsa “n’zosamvetsetseka chifukwa moyo umakhala utayambika kale.”
Asayansi apeza kuti mamolekyu a mu selo, amagwira ntchito zosiyanasiyana. Ntchito zake ndi monga kusintha chakudya kuti chikhale mphamvu, kukonza mbali za maselo zomwe zawonongeka komanso kupereka mauthenga ku selo. Ndiye kodi zingakhale zomveka kunena kuti maselo omwe amachita zinthu zonsezi anachita kusintha kuchokera ku zinthu zina? Ambiri amaona kuti zimenezi n’zosatheka.
Anthu komanso nyama zimakula kuchokera ku dzira lomwe lakumana ndi umuna. Dziralo limakhala ndi maselo ndipo maselowo amayamba kuchulukana. Zikatere, maselowo amayamba kuoneka mosiyanasiyana ndipo amapanga mbali za thupi. Koma amene amakhulupirira kuti zinthu zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina, amalephera kufotokoza kuti zimenezi zimachitika bwanji.
Panopa asayansi atulukira zoti, kuti chinthu chamoyo chisinthe n’kukhala china, pangafunike kuti mamolekyu a maselo a chinthucho asinthe. Ndiyetu zingakhale zosamveka kuti chinthu chamoyo choyambirira chinasintha pang’onopang’ono n’kukhala zamoyo zomwe timaona masiku ano. Anthu amene amakhulupirira kuti zamoyo zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina, sangafotokoze bwino mmene ngakhale selo wamba limapangidwira. Wasayansi wina dzina lake, Michael Behe anati: “Tikachita kafukufuku pa zinthu zamoyo, zimene timapeza zimakhala zodabwitsa kwambiri. Ambirife timaona kuti zimenezi sizingangochitika zokha. Payenera kuti pali winawake amene anazilenga.”
Anthu amaganiza kwambiri kuposa nyama komanso ali ndi makhalidwe monga kuwolowa manja ndiponso kudzipereka. Amathanso kudziwa zoyenera ndi zosayenera kuchita. Anthu amene amakhulupirira kuti zamoyo zinachokera ku chinthu chamoyo choyambirira chomwe chinayamba kusintha pang’onopang’ono, sangathe kufotokoza kuti zinatheka bwanji kuti anthu akhale ndi makhalidwe amenewa.
MFUNDO YAKE: Ngakhale kuti asayansi ambiri amakhulupirira kuti zamoyo zinachokera ku zinthu zina, asayansi ena sakhulupirira zimenezi. Zili choncho chifukwa zimene amanena asayansi amene amakhulupirira kuti zamoyo zinachokera ku zinthu zina, siziyankha momveka funso lakuti, kodi moyo unayamba bwanji? ndi lakuti, kodi mitundu yosiyanasiyana ya zamoyo inachokera kuti?
-
-
Baibulo Lili Ndi Mayankho Ogwira MtimaGalamukani!—2015 | January
-
-
PACHIKUTO | KODI MOYO UNAYAMBA BWANJI?
Baibulo Lili Ndi Mayankho Ogwira Mtima
ANTHU ambiri akaganizira umboni womwe ulipo amaona kuti payenera kukhala winawake wanzeru amene analenga zonse. Pulofesa wina dzina lake Antony Flew, poyamba ankalimbikitsa chikhulupiriro choti kulibe Mulungu. Kenako anaphunzira zinthu zochititsa chidwi zokhudza moyo komanso kuti zinthu zakuthambo zimayenda motsatira malamulo enaake. Zimenezi zinapangitsa kuti asinthe maganizo ake. Flew analemba mfundo yomwe akatswiri akale anzeru za anthu ankaikhulupirira. Iye anati: “Tiyenera kuvomereza zotsatira za kafukufuku ngakhale zitakhala kuti n’zosiyana ndi zomwe timayembekezera.” Pulofesayu anaona kuti kafukufuku amasonyeza kuti pali winawake wanzeru amene analenga zinthu zonse.
Gerard, yemwe tamutchula m’nkhani yoyamba ija, nayenso anayamba kukhulupirira zimenezi. Iye anati: “Ndimaona kuti palibe umboni wokhutiritsa wosonyeza kuti zamoyo zinachita kusintha kuchokera ku zinthu zina. Zamoyo zimachita zinthu mwadongosolo komanso mogometsa kwambiri. Payenera kuti pali winawake amene anazilenga chifukwa zimenezi sizingangochitika zokha.”
Munthu akhoza kudziwa zambiri za katswiri wojambula zithunzi poona zimene katswiriyo anajambula. Nayenso Gerard anayamba kudziwa makhalidwe amene Mulungu ali nawo poona zimene Mulunguyo analenga. Anaphunziranso zambiri za Mulungu kudzera m’Mawu ake, Baibulo. (2 Timoteyo 3:16) Zinthu zina zimene anaphunzira m’Baibulo ndi mfundo zomveka bwino zonena za anthu oyambirira komanso zimene munthu angachite ngati akukumana ndi mavuto. Zimenezi zinamupangitsa kutsimikizira kuti Baibulo ndi Mawudi a Mulungu.
M’Baibulo muli mayankho ogwira mtima a mafunso osiyanasiyana. Tikukulimbikitsani kuti inunso muliphunzire ndipo mudzapeza mayankho a mafunso osiyanasiyana omwe muli nawo.
-