-
Adamu ndi HavaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Ngati Wina Anena Kuti—
‘Uchimo wa Adamu unali chifuniro cha Mulungu, kakonzedwe ka Mulungu’
Mungayankhe kuti: ‘Anthu ambiri anena zimenezo. Koma ngati ine ndinafunikira kuchita kanthu kena kamene inu munafuna kuti ndichite, kodi mukanditsutsa nako kanthuko? . . . Pamenepa, ngati uchimo wa Adamu unali chifuniro cha Mulungu, kodi nchifukwa ninji Adamu anathamangitsidwa m’munda wa Edene monga wochimwa? (Gen. 3:17-19, 23, 24)’
Kapena mukanati: ‘Imeneyo iri mfundo yokondweretsa, ndipo yankho limaphatikizapodi mtundu wa munthu amene Mulungu ali. Kodi kukakhala kolungama kapena kwachikondi kutsutsa munthu kaamba ka kuchita chinthu chimene inu mwini mwamlinganizira kuti achite?’ Ndiyeno mwinamwake mungawonjezere: (1) ‘Yehova ali Mulungu wachikondi. (1 Yoh. 4:8) Njira zake zonse ndichiweruzo. (Sal. 37:28; Deut. 32:4) Sichinali chifuniro cha Mulungu kuti Adamu achimwe; iye anachenjeza Adamu kusatero. (Gen. 2:17)’ (2) ‘Mulungu analoleza Adamu, monga momwe amachitira kwa ife, ufulu wa kusankha chimene akachita. Ungwiro sunaletse kugwiritsira ntchito ufulu wa kusankha kusamvera. Adamu anasankha kupandukira Mulungu, mosasamala kanthu za chenjezo lakuti imfa ikakhala chotulukapo.’ (Wonaninso tsamba 118.)
-
-
AkaziKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Akazi
Tanthauzo: Anthu achikulire achikazi. M’Chihebri, liwu lakuti mkazi ndiro ’ish·shahʹ, limene kwenikweni limatanthauza “mwamuna wachikazi.”
Kodi Baibulo limaluluza akazi kapena kuwachitira ngati kuti anali anthu apansi?
Gen. 2:18, NW: “Yehova Mulungu anapitirizabe kunena kuti: ‘Sikuli bwino kuti mwamuna apitirizebe kukhala yekha. Ndidzampangira womthangata, monga womkwaniritsa.’” (Panopa mwamuna sakulongosoledwa ndi Mulungu kukhala munthu wabwino kwambiri kuposa mkazi. Mmalo mwake, Mulungu anasonyeza kuti mkazi akakhala ndi mikhalidwe imene ikwaniritsa ya mwamuna mkati mwa kakonzedwa ka Mulungu. Chokwaniritsa ndicho chimodzi cha zinthu ziŵiri zimene zimapanga chinthu chimodzi. Motero akazi monga kagulu ali apadera m’mikhalidwe ina ndi maluso; amuna, mu ina. Yerekezerani ndi 1 Akorinto 11:11, 12.)
Gen. 3:16: “Kwa mkaziyo ndipo [Mulungu] anati . . . udzakhumba mwamuna wako, ndipo iye adzakulamulira iwe.” (Chilengezo chimenechi chapambuyo pa kuchimwa kwa Adamu ndi Hava sichinali mawu amene amuna ayenera kuchita koma chimene Yehova anadziŵiratu kuti iwo akachita chifukwa chakuti tsopano dyera linali mbali ya moyo waumunthu. Pambuyo pa zimenezo zolembedwa zingapo Zabaibulo zimasimba za mikhalidwe yomvetsa chisoni kwambiri imene inabuka chifukwa cha ulamuliro wadyera wotero wochitidwa ndi amuna. Koma Baibulo silimanena kuti Mulungu anavomereza mkhalidwe wotero kapena kuti ndiwo chitsanzo chooti ena atsatire.)
Kodi kupatsidwa umutu kwa amuna kumachepetsa akazi?
Kukhala pansi pa umutu mwa iko kokha sikumatanthauza kuchepetsedwa. Umutu umathandizira kusamalira zinthu mwa kakonzedwe ka dongosolo, ndipo Yehova ali ‘Mulungu osati wachisokonezo, koma wamtendere.’ (1 Akor. 14:33) Yesu Kristu ali pansi pa umutu wa Yehova Mulungu, ndipo amapeza chikhutiro chachikulu muunansi umenewo.—Yoh. 5:19, 20; 8:29; 1 Akor. 15:27, 28.
Umutu wocheperapo waperekedwanso kwa mwamuna, makamaka m’banja ndi mu mpingo Wachikristu. Mulungu sanapatse mwamuna ulamuliro wotheratu pamkazi; mwamuna ayenera kuyankha ku mutu wake, Yesu Kristu, ndi kwa Mulungu kaamba ka mmene akugwiritsira ntchito umutu wotero. (1 Akor. 11:3) Ndiponso, amuna akulamulidwa kuti “azikonda akazi awo a iwo okha monga ngati matupi a iwo okha” ndi ‘kuchitira ulemu’ akazi awo. (Aef. 5:28; 1 Pet. 3:7) Zofunika zamangaŵa aukwati za mwamuna siziyenera kukhala pamwamba pa za mkazi wake m’kakonzedwe ka Mulungu kwa okwatirana. (1 Akor. 7:3, 4) Ntchito ya mkazi waluso, monga momwe yalongosoledwera m’Baibulo, imagogomezera kufunika kwake kubanja ndi ku chitaganya. Imampatsa mpata waukulu umene angagwiritsiremo ntchito luso lake pamene akusonyeza ulemu wake kaamba ka umutu wa mwamuna wake. (Miy. 31:10-31) Baibulo limalamulira ana kulemekeza osati kokha atate wawo komanso amawo. (Aef. 6:1-3) Limaperekanso chisamaliro chapadera ku kusamalira zosoŵa za akazi amasiye. (Yak. 1:27) Motero pakati pa Akristu owona, akazi angadzipezere chitetezo chachikulu, ulemu wowona kaamba ka iwo eni monga anthu, ndi chikhutiro chawo muutumiki wawo.
Kulemekezeka kwa malo antchito a mkazi m’kakonzedwe ka Mulungu kwasonyezedwanso ndi chenicheni chakuti Yehova amatchula gulu lake la zolengedwa zauzimu zokhulupirika monga mzimayi, mkazi wake, mayi wa ana ake. (Chiv. 12:1; Agal. 4:26) Ndiponso, mpingo wa odzozedwa ndi mzimu wa Yesu Kristu umalankhulidwa monga mkwatibwi wake. (Chiv. 19:7; 21:2, 9) Ndipo m’lingaliro lauzimu palibe kusiyana pakati pa mwamuna ndi mkazi pakati pa oitanidwira kukhala ndi phande mu Ufumu wakumwamba limodzi ndi Kristu.—Agal. 3:26-28.
Kodi akazi ayenera kukhala aminisitala?
Awo opatsidwa uyang’aniro wampingo amafotokozedwa m’Baibulo kukhala amuna. Atumwi onse 12 a Yesu Kristu anali amuna, ndipo awo amene pambuyo pake anaikidwa kukhala oyang’anira ndi atumiki otumikira m’mipingo Yachikristu anali amuna. (Mat. 10:1-4; 1 Tim. 3:2, 12) Akazi amalangizidwa ‘kuphunzira ali chete ndi chigonjero chokwanira’ pamisonkhano yampingo, m’chakuti samadzutsa mafunso otsutsana ndi amuna mu mpingo. Akazi ‘sayenera kulankhula’ pamisonkhano yotero ngati zimene anganene zingasonyeze kusagonjera. (1 Tim. 2:11, 12; 1 Akor. 14:33, 34) Motero, ngakhale kuli kwakuti akazi akuthandizira kwambiri ntchito yampingo, palibe kakonzedwe kakuti iwo atsogoze, kapena kutsogolera mwa kulangiza mpingo, pamene amuna oyeneretsedwa alipo.
Koma kodi akazi angakhale alaliki, olengeza, aminisitala a mbiri yabwino, kunja kwa misonkhano yampingo? Pa Pentekoste wa 33 C.E. mzimu woyera unatsanuliridwa pa onse amuna ndi akazi omwe. Polongosola, mtumwi Petro anagwira mawu Yoweli 2:28, 29 kumati: “Kudzali m’masiku otsiriza, anena Mulungu, ndidzathira chamzimu wanga pathupi lirilonse, ndipo ana anu aamuna ndi akazi adzanenera, ndipo anyamata anu adzawona masomphenya, ndi akulu anu adzalota maloto; ndiponso pa akapolo anga ndi pa adzakazi anga m’masiku awa, ndidzathira chamzimu wanga; ndipo adzanenera.” (Mac. 2:17, 18) Mofananamo, akazi lerolino moyenelera amakhala ndi phande muuminisitala Wachikristu, kulalikira kunyumba ndi nyumba ndi kuchititsa maphunziro Abaibulo apanyumba.—Wonaninso Salmo 68:11; Afilipi 4:2, 3.
Kodi nchifukwa ninji Akazi Achikristu amavala chophimba kumutu panyengo zina?
1 Akor. 11:3-10: “Mutu wa munthu yense ndiye Kristu; ndi mutu wamkazi ndiye mwamuna; ndipo mutu wa Kristu ndiye
-