-
AyudaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
bwalo, ndi kusanduliza dzikoli kukhala phata la demokrase.”)
Zek. 8:23, JP: “Kudzali m’masiku awo, kuti amuna khumi adzagwira, ochokera m’zinenero zonse za amitundu, adzagwiradi mkawo wa iye amene ali Myuda, akumati: Tidzamka nanu, pakuti tamva kuti Mulungu ali ndi inu.” (Kodi ulosiwu ukusonya kwa Mulungu uti? M’chinenero Chachihebri dzina lake [יהוה, limene kaŵirikaŵiri latembenuzidwa kukhala Yehova] limawonekera zoposa nthaŵi 130 m’bukhu limodzi lokha iri la Malemba Opatulika. Lerolino pamene munthu wina agwiritsira ntchito dzina limenelo, kodi anthu amanena kuti munthuyo ayenera kukhala Myuda? Ayi; kwa zaka mazana ambiri, kukhulupirira malaulo kwachititsa anthu onse Achiyuda kupeŵa kutchula kulikonse dzina laumwini la Mulungu. Kukula kwa mwadzidzidzi kwa kukondweretsedwa ndi chipembedzo lerolino kophatikizapo Israyeli wakuthupi sikumayenerana ndi malongosoledwe a ulosiwu.)
Pamenepa, kodi ndimotani, mmene zochitika mu Israyeli wamakono ziyenera kuwonedwera? Monga mbali chabe ya zochitika zapadziko lonse zonenedweratu m’Baibulo. Zimenezi zikuphatikizapo nkhondo, kusayeruzika, kuzirala kwa kukonda Mulungu, ndi kukonda ndalama.—Mat. 24:7, 12; 2 Tim. 3:1-5.
Kodi maulosi onena za kubwezeretsedwa kwa Israyeli akwaniritsidwa pakati pa ayani lerolino?
Agal. 6:15, 16, NW: “Pakuti mdulidwe suuli kanthu kusadulidwanso sikuli kanthu, koma kulengedwa kwatsopano ndiko kuli kanthu. Ndipo awo onse amene atsatira chilangizo ichi, mtendere ndi chifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israyeli wa Mulungu.” (Chotero “Israyeli wa Mulungu” samatsimikiziridwanso pamaziko a kuchita mogwirizana nchofunika chotchulidwa kwa Abrahamu kaamba ka amuna onse abanja lake cha kudulidwa. Mmalo mwake, monga momwe kwafotokozedwera pa Agalatiya 3:26-29, awo amene ali a Kristu ndi ana obadwa ndi mzimu a Mulungu “alidi mbewu ya Abrahamu.”)
Yer. 31:31-34: “Tawonani, masiku adza, ati Yehova, ndipo ndidzapangana pangano latsopano ndi nyumba ya Israyeli, ndi nyumba ya Yuda; . . . ndipo sadzaphunzitsa yense mnansi wake, ndi yense mbale wake, kuti, Mudziŵe Yehova; pakuti iwo onse adzandidziŵa, kuyambira wamng’ono kufikira wamkulu wa iwo, ati Yehova.” (Pangano latsopano limenelo linapangidwa, osati ndi mtundu wa Israyeli wakuthupi, koma ndi otsatira okhulupirika a Yesu Kristu amene anapatsidwa chiyembekezo cha moyo kumwamba. Poyambitsa Chikumbutso cha imfa yake, Yesu anawapatsa chikho cha vinyo ndipo anati: “Chikho ichi ndipangano latsopano m’mwazi wanga.” [1 Akor. 11:25])
Chiv. 7:4: “Ndinamva chiŵerengero cha iwo osindikizidwa chizindikiziro, zikwi makumi khumi ndi makumi anayi mphambu anayi, osindikizidwa chizindikiro mwa mafuko onse a ana a Israyeli.” (Koma m’mavesi otsatira, mwatchulidwa “fuko la Levi” ndi “fuko la Yosefe.” Amenewa sanaphatikizidwe m’ndandanda zamafuko 12 a Israyeli wakuthupi. Mokondweretsa, pamene kuli kwakuti kukunenedwa kuti anthu “akasindikizidwa chizindikiro mwa mafuko onse a ana a Israyeli,” fuko la Dani ndi fuko la Efraimu silikutchulidwa. [Yerekezerani ndi Numeri 1:4-16.] Panopa otchulidwawo ayenera kukhala Israyeli wauzimu wa Mulungu, kwa awo amene Chivumbulutso 14:1-3 chimasonyeza kuti adzakhala ndi phande limodzi ndi Kristu mu Ufumu wake wakumwamba.)
Aheb. 12:22: “Mwayandikira ku Phiri la Ziyoni, ndi mudzi wa Mulungu wa moyo, Yerusalemu wakumwamba, ndi kwa unyinji wochuluka wa angelo.” (Chotero sikuli ku Yerusalemu wapadziko lapansi koma ku “Yerusalemu wakumwamba” kumene Akristu owona amayang’anako kaamba ka kukwaniritsidwa kwa malonjezo a Mulungu.)
-
-
Babulo WamkuluKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Babulo Wamkulu
Tanthuzo: Ulamuliro wa dziko lonse wa chipembedzo chonyenga, wophatikizapo zipembedzo zonse zimene ziphunzitso zake ndi zizoloŵezi sizimagwirizana ndi kulambiridwa kowona kwa Yehova, Mulungu wowona yekha. Pambuyo pa chigumula cha tsiku la Nowa, chipembedzo chonyenga chinayambira pa Babele (pambuyo pake wodziŵika monga Babulo). (Gen. 10:8-10; 11:4-9) M’nthaŵi yokwanira, zikhulupiriro za chipembedzo cha Babulo zinafikira ku maiko ambiri. Chotero Babulo Wamkulu linafikira kukhala dzina loyenerera la chipembedzo chonse chonyenga.
Kodi ndiumboni wotani umene umasonya kukudziŵikitsidwa kwa Babulo Wamkulu, wotchulidwa m’Chivumbulutso?
Sukanakhala mzinda wakale wa Babulo. Chivumbulutso
-