Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 20-21
  • Yerusalemu ndi Kachisi wa Solomo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yerusalemu ndi Kachisi wa Solomo
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 20-21

Yerusalemu ndi Kachisi wa Solomo

Mzinda wa Davide

ANKATCHEDWA ‘wokongola mwangwiro’ komanso ‘mudzi wa Mfumu yaikulu.’ (Sal. 48:2; 50:2; Maliro 2:15) Yerusalemu anali likulu la mtundu wa Mulungu. (Sal. 76:2) Davide ataulanda kwa Ayebusi n’kuikako likulu lake, mudziwu unayamba kutchedwa “mudzi wa Davide,” kapena kungoti “Ziyoni.”—2 Sam. 5:7.

Ngakhale kuti sanali pamalo abwino kwenikweni, Yerusalemu anatchuka chifukwa chakuti Mulungu anaikako dzina lake. (Deut. 26:2) Anali likulu la chipembedzo ndiponso likulu la boma la mtundu wa Israyeli.

Yerusalemu ali pamalo okwera mamita 750 m’katikati mwa mapiri a Yudeya. Baibulo limafotokoza za “phiri” lake ndipo limati olambira ankachita ‘kukwera’ kuti akafikepo. (Sal. 48:2; 122:3, 4) Mudzi wakalewu unazunguliridwa ndi zigwa: kumadzulo ndi kum’mwera kwake kunali Chigwa cha Hinomu ndipo kum’maŵa kwake kunali chigwa cha Kidroni. (2 Maf. 23:10; Yer. 31:40) Mudziwu unkapeza madzi abwino pa akasupe a Gihonia m’Chigwa cha Kidroni ndi Eni-rogeli kumadzulo kwake, ndipo akasupeŵa anali ofunika kwambiri makamaka adani akauukira mudziwu.—2 Sam. 17:17.

Yerusalemu/Kachisi wa Solomo

Pachithunzi chomwe chili patsamba 21, Mudzi wa Davide ndi wofiirawo. Mu ulamuliro wa Davide ndi Solomo, mudziwu unakula kuloŵera kumpoto n’kukaphatikiza Ofeli (dera lagirini) ndi Phiri la Moriya (dera labluu). (2 Sam. 5:7-9; 24:16-25) Solomo anamangira Yehova kachisi wokongola kwambiri pamalo okwera a paphiri limeneli. Tayerekezerani kuti mukuona anthu miyandamiyanda akukhamukira ku “phiri la Yehova” kudzachita mapwando apachaka! (Zek. 8:3) Maulendo oterowo anali osavuta chifukwa cha misewu yomwe yasonyezedwa patsamba 17.

Kachisi wa Solomo, yemwe anam’kongoletsa ndi golide ndiponso miyala ina yamtengo wapatali, anali imodzi mwa nyumba zomwe zamangidwa ndi ndalama zambiri. Yehova ndiye anakonza mapulani ake, ndipo zimenezi zili ndi tanthauzo kwambiri. Monga momwe mukuonera pachithunzipa, kachisiyu anali ndi mabwalo akuluakulu ndiponso nyumba zaboma zikuluzikulu kumbali yake inayo. Ndi bwino kuphunzira zinthu zosiyanasiyana zokhudza kachisiyu.—1 Maf. 6:1–7:51; 1 Mbiri 28:11-19; Aheb. 9:23, 24.

[Mawu a M’munsi]

a Mfumu Hezekiya anatseka kasupeyu n’kukumba ngalande yokafika kudziŵe la kumadzulo kwa mudziwu.—2 Mbiri 32:4, 30.

[Bokosi patsamba 21]

M’kupita kwa nthaŵi, Yerusalemu anakula kuloŵera kumadzulo ndi kumpoto. Mafumu a Yuda olamulira pambuyo pa Solomo anawonjezera malinga ake ndi zipata zake. Kufukula za m’mabwinja komwe kuli m’kati kungathandize kudziŵa malo ake enieni a mbali zina za malingawo ndi kumene anadutsa. Mzindawu unawonongedwa mu 607 B.C.E. ndipo unakhala bwinja zaka 70. Patatha zaka pafupifupi 80 Ayuda atabwerera kwawo, Nehemiya anayamba ntchito yaikulu yomanganso malinga a Yerusalemu.

[Chithunzi patsamba 21]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Yerusalemu/Kachisi wa Solomo

MALO A KACHISI M’NTHAŴI YA SOLOMO

Mbali za Kachisi

1. Malo Opatulikitsa

2. Malo Opatulika

3. Likole

4. Boazi

5. Yakini

6. Guwa la Nsembe Lamkuwa

7. Thaŵale Lamkuwa

8. Maphaka

9. Zipinda za M’mbali

10. Zipinda Zodyera

11. Bwalo Lamkati

MALO A KACHISI

Phiri la Moriya

Zipinda Zodyera

Maphaka

Zipinda za M’mbali

Malo Boazi

Opatulikitsa Malo Opatulika Guwa la Nsembe Bwalo

Yakini Lamkuwa Lamkati

Maphaka Thaŵale

Lamkuwa

Ofeli

Bwalo la Kuchipata?

Chipata cha Kumadzi?

MUDZI WA DAVIDE

Phiri la Ziyoni

Nyumba Yachifumu ya Davide

Chipata cha Chitsime

Linga la Manase?

Nsanja ya Hananeeli

Nsanja ya Mea

Chipata cha Nkhosa

Chipata cha Kaidi

Chipata cha Hamifikadi

Chipata cha Akavalo

CHIGWA CHA KIDRONI

Linga la Kunsi?

Gihoni

Ngalande yomwe anadzakumba

CHIGWA CHA TYROPOEON

Chipata cha Kudzala (Mapale) (Ndowe)

Eni-rogeli

Chipata cha Kuchigwa

CHIGWA CHA HINOMU

Chipata cha Kungondya

Nsanja ya Ng’anjo

Linga Lachitando

Chipata cha Efraimu

Bwalo la Kuchipata

Chipata cha Mudzi Wakale

Linga Lakale Lakumpoto

DERA LACHIŴIRI

Chipata cha Nsomba

[Chithunzi]

Ofeli

Nyumba ya Mwana Wamkazi wa Farao

Nyumba Yachifumu ya Solomo

Nyumba ya Nkhalango ya Lebano

Khumbi la Nsanamira

Khumbi la Mpando Wachifumu

Phiri la Moriya

Bwalo Lalikulu

Kachisi

[Chithunzi patsamba 20]

Pachithunzipa, “Mudzi wa Davide” unali chakuno. Kachisi anali pamalo afulati (kutsogoloko)

[Chithunzi patsamba 20]

Chithunzi chopanga pakompyuta cha “Mudzi wa Davide” wakale ndi kachisi wa Solomo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena