Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp17 No. 1 tsamba 3
  • Kodi Ubwino Wowerenga Baibulo Ndi Wotani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ubwino Wowerenga Baibulo Ndi Wotani?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Mungatani Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzikuthandizani Kwambiri?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Ndingatani Kuti Kuŵerenga Baibulo Kuzindisangalatsa?
    Galamukani!—2001
  • Chitani Khama pa Kuŵerenga
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Ndiziwerenga Chifukwa Chiyani?
    Galamukani!—2006
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
wp17 No. 1 tsamba 3
Mayi akutenga Baibulo pashelefu

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUNGATANI KUTI KUWERENGA BAIBULO KUZIKUSANGALATSANI?

Kodi Ubwino Wowerenga Baibulo Ndi Wotani?

“Ndinkaganiza kuti Baibulo ndi lovuta kumvetsa.”—Jovy

“Ndinkaona ngati nkhani zake n’zotopetsa.”—Queennie

“Ndinkaona kuti Baibulo ndi lalikulu kwambiri moti sindinkafuna n’komwe kuliwerenga.”—Ezekiel

Kodi munaganizapo zowerenga Baibulo koma kenako n’kugwa ulesi mofanana ndi anthu amene tawatchula pamwambawa? Anthu ambiri amaona kuti sangakwanitse kuwerenga Baibulo. Koma kodi mungafune kuliwerenga mutadziwa kuti likhoza kukuthandizani kukhala ndi moyo wosangalala? Nanga mungamve bwanji mutadziwa kuti pali zinthu zimene zingakuthandizeni kuti kuwerenga Baibulo kuzikusangalatsani?

Taonani zimene anthu ena ananena atayamba kuwerenga Baibulo n’kuona ubwino wake.

Ezekiel, yemwe ndi wazaka za m’ma 20, anati: “Poyamba ndinkachita zinthu ngati munthu amene akuyendetsa galimoto popanda kwenikweni kumene akupita. Koma kuwerenga Baibulo kwandithandiza kukhala ndi moyo wabwino chifukwa lili ndi malangizo amene amandithandiza tsiku ndi tsiku.”

Mtsikana wina dzina lake Frieda, yemwenso ndi wazaka za m’ma 20, ananena kuti: “Sindinkachedwa kuyambana ndi anzanga. Koma panopa ndimatha kuugwira mtima chifukwa chowerenga Baibulo. Zimenezi zandithandiza kuti ndisamavutike kugwirizana ndi anthu ena, moti panopa ndili ndi anzanga ambiri.”

Mayi wina wazaka za m’ma 50, dzina lake Eunice, anati: “Baibulo landithandiza kukhala ndi makhalidwe abwino ndiponso kusiya zinthu zoipa.”

Baibulo lingakuthandizeni kukhala ndi moyo wosangalala mofanana ndi mmene lathandizira anthu amene tawatchulawa komanso anthu ena ambiri. (Yesaya 48:17, 18) Mwachitsanzo, likhoza kukuthandizani kusankha zinthu mwanzeru, kupeza anzanu abwino, kuchepetsa nkhawa ndiponso kuphunzira mfundo zoona zokhudza Mulungu, chomwe ndi chinthu chofunika kwambiri. Malangizo a m’Baibulo amachokera kwa Mulungu ndipo sangakugwiritseni fuwa la moto. Zili choncho chifukwa Mulungu sangapereke malangizo olakwika.

Koma kodi ndi zinthu ziti zimene zingakuthandizeni kuyamba kuwerenga Baibulo komanso kusangalala poliwerenga?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena