Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 10 tsamba 30
  • Kumbukirani Mkazi wa Loti

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kumbukirani Mkazi wa Loti
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mkazi wa Loti Anacheuka
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Konzekerani Kaamba ka Chipulumutso Kuloŵa M’dziko Latsopano
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Mulungu Anachita Pangano ndi Abulahamu
    Kodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
  • Tizithandiza Anthu Amene Ali ndi Nkhawa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 10 tsamba 30
Mkazi wa Loti wasanduka chipilala cha mchere pamene Loti ndi ana ake aakazi akutuluka mu Sodomu

MUTU 10

Kumbukirani Mkazi wa Loti

Loti ankakhala ndi Abulahamu ku Kanani. Lotiyu anali mwana wa mng’ono wake wa Abulahamu. Kenako onse anakhala ndi ziweto zambiri moti malo odyetsera ziwetozo anawachepera. Ndiyeno Abulahamu anauza Loti kuti: ‘N’zosatheka kuti tizikhalabe limodzi. Yamba iweyo kusankha kumene ukufuna kukakhala ndipo ine ndipita kwinako.’ Apatu Abulahamu anasonyeza kuti sanali wodzikonda.

Loti anaona dera lapafupi ndi mzinda wa Sodomu limene linali lokongola. Iye anakopeka ndi derali chifukwa linali ndi madzi ambiri komanso udzu wobiriwira. Choncho anasankha dera limeneli ndipo anasamukira kumeneku ndi banja lake.

Anthu a mumzinda wa Sodomu komanso mzinda wina wapafupi wotchedwa Gomora anali ndi makhalidwe oipa kwambiri. Choncho Yehova anaona kuti ndi bwino kungowononga mizindayo. Koma Mulungu anaganiza zoti apulumutse Loti ndi banja lake. Iye anatumiza angelo awiri kukawauza kuti: “Fulumirani! Tulukani mumzinda uno, chifukwa Yehova auwononga.”

Koma Loti ndi banja lake ankangochedwachedwa moti angelowo anachita kuwagwira manja n’kuwatulutsa mumzindawo. Iwo anawauza kuti: ‘Thawani mupulumutse moyo wanu! Musayangʼane kumbuyo chifukwa mukangoyang’ana mufa.’

Moto ndi sulufule zikugwera pa mzinda wa Sodomu ndi Gomora

Iwo atafika mumzinda wa Zowari, Yehova anagwetsa moto ndi sulufule ngati mvula mumzinda wa Sodomu ndi Gomora. Mizinda yonseyi inapseratu. Koma mkazi wa Loti sanamvere Yehova ndipo anayang’ana m’mbuyo. Atangotero anasanduka chipilala chamchere. Komabe Loti ndi ana ake aakazi anapulumuka chifukwa choti anamvera Yehova. Onse ayenera kuti anamva chisoni ataona kuti mayi afa chifukwa chosamvera. Koma anasangalala kuti iwowo anamvera malangizo a Yehova.

“Kumbukirani mkazi wa Loti.”​—Luka 17:32

Mafunso: N’chifukwa chiyani Yehova anawononga mzinda wa Sodomu ndi Gomora? N’chifukwa chiyani mkazi wa Loti anasanduka chipilala chamchere?

Genesis 13:1-13; 19:1-26; Luka 17:28, 29, 32; 2 Petulo 2:6-9

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena