-
Mose Anasankha Kuti Azilambira YehovaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 17
Mose Anasankha Kuti Azilambira Yehova
Ku Iguputo, anthu a m’banja la Yakobo anayamba kudziwika kuti Aisiraeli. Yakobo ndi Yosefe atamwalira, Farao wina anayamba kulamulira. Iye ankachita mantha chifukwa Aisiraeli anali amphamvu kuposa Aiguputo. Choncho Farao ameneyu anachititsa kuti Aisiraeli akhale akapolo. Anawalamula kuti aziumba njerwa komanso kugwira ntchito zotopetsa kumunda. Koma ngakhale kuti ankazunzidwa kwambiri ndi Aiguputo, Aisiraeli anapitirizabe kuchulukana. Popeza Farao sankafuna zimenezi, analamula kuti ana onse aamuna a Aisiraeli aziphedwa akangobadwa. Ukuganiza kuti Aisiraeli anamva bwanji lamuloli litaperekedwa?
Izi zitachitika, mayi wina wa Chiisiraeli, dzina lake Yokebedi anabereka mwana wamwamuna wokongola kwambiri. Pofuna kuteteza mwanayo, mayiyo anamuika m’basiketi n’kukamubisa m’mabango, mumtsinje wa Nailo. Mchemwali wake wa mwanayo, dzina lake Miriamu, anakhala chapafupi kuti azimuyang’anira.
Ndiyeno mwana wamkazi wa Farao anabwera kuti adzasambe ndipo anaona basiketi ija. Atatsegula basiketiyo anapeza kuti munali mwana. Mwanayo ankalira ndipo anamumvera chisoni. Miriamu anafunsa mwana wamkazi wa Faraoyo kuti: ‘Kodi mungakonde kuti ndikakufufuzireni mzimayi woti azimusamalira?’ Mwana wa Farao atavomera, Miriamu anapita n’kukauza amayi ake, a Yokebedi. Atabwera, mwana wa Faraoyo anawauza kuti: ‘Tengani mwanayu, muzikamusamalira ndipo ndizikulipirani.’
Mwana uja atakula, Yokebedi anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anamupatsa dzina loti Mose n’kumakhala naye ngati mwana wake. Mose analeredwa ngati mwana wa mfumu ndipo akanatha kupeza chilichonse chimene ankafuna. Koma iye sanaiwale Yehova. Ankadziwa kuti anali wa ku Isiraeli osati wa ku Iguputo ndipo anasankha kuti azitumikira Yehova.
Ali ndi zaka 40, Mose ankafuna kuthandiza Aisiraeli anzake. Choncho ataona munthu wa ku Iguputo akumenya munthu wa Chiisiraeli, Mose anamenya munthu wa ku Iguputoyo mpaka kumupha. Atatero anakwirira munthu wakufayo mumchenga. Farao atadziwa zimenezi, ankafuna kupha Mose. Choncho Mose anathawira ku Midiyani. Kumeneko, Yehova anali naye.
“Chifukwa cha chikhulupiriro, Mose . . . anakana kutchedwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao, ndipo anasankha kuzunzidwa limodzi ndi anthu a Mulungu.”—Aheberi 11:24, 25
-
-
Anaona Chitsamba ChikuyakaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 18
Anaona Chitsamba Chikuyaka
Mose anakhala ku Midiyani kwa zaka 40. Iye anakwatira n’kukhala ndi ana. Tsiku lina akudyetsa nkhosa pafupi ndi phiri la Sinai, anaona zinthu zodabwitsa. Anaona chitsamba chikuyaka koma sichinkapsa. Atayandikira kuti aone zimene zikuchitika, anamva mawu ochokera m’chitsambacho akuti: ‘Mose! Usayandikire kuno. Vula nsapato zakozo chifukwa malo amene waimawo ndi oyera.’ Yehova ndi amene ankamulankhula ndipo anagwiritsa ntchito mngelo.
Mose anachita mantha kwambiri moti anaphimba nkhope yake. Yehova anamuuza kuti: ‘Ndaona kuti Aisiraeli akuvutika kwambiri. Ndikufuna kuwapulumutsa ku Iguputo n’kuwapititsa kudziko labwino. Iweyo ndi amene uwatsogolere pochoka ku Iguputo.’ Mose ayenera kuti anadabwa kwambiri ndi zimenezi.
Iye anafunsa kuti: ‘Nanga akakandifunsa kuti wakutuma ndi ndani, ndikayankhe kuti chiyani?’ Mulungu anamuuza kuti: ‘Ukawauze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo, ndi amene wandituma kwa inu.’ Kenako Mose anati: ‘Nanga akakapanda kundimvera?’ Yehova anapatsa Mose umboni womutsimikizira kuti adzamuthandiza. Yehova anamuuza kuti aponye ndodo yake pansi. Nthawi yomweyo ndodoyo inasanduka njoka. Koma ataigwira kumchira, inasandukanso ndodo. Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: ‘Ukakachita zimenezi, akakhulupirira kuti ndakutumadi.’
Koma Mose anati: ‘Pajatu ine ndimavutika kulankhula.’ Ndiyeno Yehova anamulonjeza kuti: ‘Ineyo ndizikakuuza zoyenera kunena ndipo ndikupatsa m’bale wako Aroni kuti azikakuthandiza.’ Mose atadziwa kuti Yehova amuthandiza, anatenga mkazi ndi ana ake n’kuyamba ulendo wopita ku Iguputo.
“Musadzade nkhawa kuti mudzalankhula bwanji kapena kuti mudzanena chiyani, chifukwa zoti mulankhule mudzapatsidwa nthawi yomweyo.”—Mateyu 10:19
-
-
Miliri Itatu YoyambiriraZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 19
Miliri Itatu Yoyambirira
Aiguputo ankaumiriza Aisiraeli kuti azigwira ntchito ngati akapolo. Yehova anatumiza Mose ndi Aroni kwa Farao kukanena kuti: ‘Yehova akuti mulole kuti anthu ake apite kuchipululu kuti akamulambire.’ Koma Farao anayankha mwamwano kuti: ‘Zimene Yehova wanenazo ndilibe nazo ntchito. Sindilola kuti Aisiraeli apite.’ Atatero anawonjezera ntchito zimene Aisiraeli ankagwira. Choncho Yehova anafuna kuti Farao adziwe kuti iye ndi wamkulu kuposa milungu yonse. Kodi ukudziwa zimene anachita? Anabweretsa Miliri 10 ku Iguputo. Yehova anauza Mose kuti: ‘Farao sakufuna kundimvera. Mawa m’mawa akhala ali kumtsinje wa Nailo. Upite ukamuuze kuti popeza sakufuna kuti anthu anga apite, madzi onse a mumtsinje wa Nailo asanduka magazi.’ Mose anamvera Yehova ndipo anapitadi kwa Farao. Kumeneko Aroni anamenya ndi ndodo madzi a mumtsinje wa Nailo, Farao akuona ndipo madziwo anasanduka magazi. Madziwo anayamba kununkha, nsomba zonse zinafa ndipo anthu anasowa madzi akumwa. Koma Farao sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
Patatha masiku 7, Yehova anatumanso Mose kwa Farao kukamuuza kuti: ‘Ukapanda kulola kuti anthu anga apite, m’dziko la Iguputo mudzakhala achule paliponse.’ Aroni anakweza ndodo yake m’mwamba ndipo achule anayamba kudzaza m’dziko lonse. Achulewo ankapezeka m’nyumba, pabedi, m’mbale, tingoti paliponse. Zitatero Farao anauza Mose kuti akapemphe kwa Yehova kuti mliriwu uthe ndipo analonjeza kuti alola Aisiraeli kuti apite. Choncho Yehova anathetsadi mliriwo ndipo achulewo anayamba kufa. Aiguputo anaunjika achulewo milumilu moti dziko lonse linkanunkha. Koma Farao ataona kuti mliri watha, sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: ‘Aroni amenye pansi ndi ndodo ndipo fumbi lisanduka tizilombo toyamwa magazi.’ Aroni anachitadi zimenezi ndipo paliponse panagwa tizilombo toyamwa magazi. Aiguputo ena anauza Farao kuti: ‘Mliriwu wachokera kwa Mulungu.’ Koma Farao sanalolebe kuti Aisiraeli apite.
“Ndiwachititsa kuti adziwe mphamvu ndi nyonga zanga, ndipo adziwa kuti dzina langa ndine Yehova.”—Yeremiya 16:21
-
-
Miliri Inanso 6Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 20
Miliri Inanso 6
Mose ndi Aroni anapita kwa Farao kukamuuza uthenga wochokera kwa Mulungu, wakuti: ‘Ngati sulola kuti anthu anga apite, nditumiza ntchentche zoluma m’dzikoli.’ Ndiyeno ntchentche zolumazo zinadzaza m’nyumba za Aiguputo onse, olemera ndi osauka omwe moti zinali mbwee paliponse. Koma ku Goseni kumene Aisiraeli ankakhala kunalibe ntchentchezi. Kuyambira ndi mliri wa nambala 4 umenewu, miliriyi inkangokhudza Aiguputo okha. Choncho Farao anachonderera Mose kuti: ‘Ukandipemphere kwa Yehova kuti achotse ntchentchezi. Zikatero ndikulolani kuti mupite.’ Koma Yehova atangochotsa ntchentchezo, Farao anasintha maganizo. Iye sanaphunzirepo kanthu.
Yehova anati: ‘Farao akapanda kulola kuti anthu anga apite, ziweto zonse za Aiguputo ziyamba kudwala n’kufa.’ Tsiku lotsatira, ziweto za Aiguputo zinayamba kufa. Koma ziweto za Aisiraeli sizinafe. Ngakhale zinali choncho, Farao sanalolebe kuti Aisiraeli azipita.
Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti apitenso kwa Farao ndipo akaponye phulusa m’mwamba. Phulusalo linasanduka fumbi ndipo linadzaza dziko lonselo moti Aiguputo onse anali fumbi lokhalokha. Fumbilo likagwera munthu kapena ziweto, linkayambitsa zilonda zopweteka kwambiri. Komabe Farao sanalole kuti Aisiraeli apite.
Yehova anatuma Mose kuti apitenso kwa Farao n’kukanena kuti: ‘Kodi sukufunabe kuti anthu anga apite? Mawa ndibweretsa mvula yamphamvu kwambiri yamatalala.’ Tsiku lotsatira, Yehova anabweretsa mvula yamatalala, mabingu ndi moto. Ku Iguputo kunali kusanagwepo chimvula ngati chimenecho chiyambire. Chimvulacho chinawononga mitengo komanso mbewu zonse kupatulapo za ku Goseni. Farao anati: ‘Kandipemphere kwa Yehova kuti aletse chimvulachi ndipo ndikulolani kuti muzipita.’ Koma matalalawo ndi chimvulacho zitangosiya, Farao anasinthanso maganizo.
Kenako Mose anati: ‘Tsopano kugwa dzombe ndipo lidya zomera zonse zimene sizinawonongedwe ndi matalala.’ Choncho kunagwa dzombe lambiri moti linadya mbewu zonse komanso masamba onse a mitengo. Farao anachondereranso kuti: ‘Kandipemphere kwa Yehova kuti achotse dzombeli.’ Koma Yehova atachotsa dzombelo, Farao anakanabe kulola kuti Aisiraeli apite.
Yehova anauza Mose kuti: ‘Tambasula dzanja lako ndipo uloze kumwamba.’ Nthawi yomweyo, kunachita mdima wandiweyani. Kwa masiku atatu, Aiguputo sankatha kuona munthu aliyense kapena chinthu chilichonse. Koma m’nyumba za Aisiraeli munkawala.
Zitatero Farao anauza Mose kuti: ‘Pitani, koma ziweto zanu muzisiye.’ Koma Mose anati: ‘Tizitenga chifukwa tikufuna kukapereka nsembe kwa Mulungu wathu.’ Farao anakwiya kwambiri n’kunena kuti: ‘Choka! Ndisadzakuonenso. Ndipo ukadzangobweranso ndidzakupha.’
“Mudzaonanso kusiyana pakati pa munthu wolungama ndi woipa ndiponso pakati pa munthu amene akutumikira Mulungu ndi amene sakumutumikira.”—Malaki 3:18
-
-
Mliri wa 10Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 21
Mliri wa 10
Mose anauza Farao kuti sadzapitanso kukaonana naye. Koma asananyamuke, anamuuza kuti: ‘Lero pakati pa usiku ana onse aamuna oyamba kubadwa a Aiguputo afa, kuyambira mwana wa Farao mpaka ana a akapolo.’
Yehova anauza Aisiraeli kuti adye chakudya chapadera. Anawauza kuti: ‘Mupeze mwana wankhosa kapena wambuzi. Akhale wamphongo komanso wachaka chimodzi. Mumuphe ndipo magazi ake mupake pamafelemu a zitseko zanu. Nyama yakeyo muiwotche ndipo muidye limodzi ndi mikate yopanda zofufumitsa. Mudye mutavala zovala zanu komanso nsapato pokonzekera ulendo. Usiku wa lero mutuluka mu Iguputo.’ Kodi ukuganiza kuti Aisiraeli anamva bwanji atauzidwa zimenezi?
Pakati pa usiku, mngelo wa Yehova anapita kunyumba zonse za mu Iguputo. Nyumba iliyonse imene inalibe magazi pafelemu, mwana woyamba anafa. Koma mngeloyo sankapha ana a m’nyumba zimene anapaka magazi pamafelemu. M’banja lililonse la Aiguputo, kaya lolemera kapena losauka, munafa mwana woyamba. Koma palibe mwana ngakhale mmodzi wa Aisiraeli amene anafa.
Mwana woyamba wa Farao weniweniyo anafanso. Apa m’pamene makani a Farao anathera. Nthawi yomweyo anauza Mose ndi Aroni kuti: ‘Nyamukani. Chokani kuno. Pitani mukalambire Mulungu wanu. Mutengenso ziweto zanu n’kumapita.’
Usiku womwewo, Aisiraeli ananyamuka ndipo kunja kunali kukuwala kwambiri chifukwa mwezi unali wathunthu. Mabanja komanso mafuko ankayendera limodzi. Panali amuna 600,000 komanso akazi ndi ana ambiri. Panalinso anthu a mitundu ina amene anapita nawo kuti akalambirenso Yehova. Apa m’pamene panathera ukapolo wa Aisiraeli.
Pofuna kukumbukira zimene Yehova anachita powapulumutsa, Aisiraeliwa ankadya chakudya chapadera chija chaka chilichonse. Mwambowu ankautchula kuti Pasika.
“Ndakusiya ndi moyo kuti ndikusonyeze mphamvu zanga komanso kuti dzina langa lilengezedwe padziko lonse lapansi.”—Aroma 9:17
-
-
Pa Nyanja Yofiira Panachitika Zodabwitsa KwambiriZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 22
Zodabwitsa Zimene Zinachitika pa Nyanja Yofiira
Farao atamva kuti Aisiraeli achoka ku Iguputo, anasintha maganizo. Anauza asilikali ake kuti: ‘Tengani magaleta anga ankhondo, tiwatsatire. Sitimayenera kuwalola kuti apite.’ Choncho Farao ndi asilikali ake anayamba kuthamangira Aisiraeli.
Yehova ankatsogolera anthu ake. Masana ankagwiritsira ntchito mtambo ndipo usiku ankagwiritsa ntchito moto. Aisiraeliwo atafika pa Nyanja Yofiira, Yehova anawauza kuti amange misasa.
Kenako Aisiraeli anaona Farao ndi asilikali ake akuwathamangira. Analibe kothawira chifukwa kutsogolo kwawo kunali nyanja ndipo kumbuyo kwawo n’kumene kunali asilikaliwo. Iwo anachita mantha kwambiri ndipo analirira Mose kuti: ‘Tifa basi! Bola ukanangotisiya ku Iguputo konkuja.’ Koma Mose anawauza kuti: ‘Musachite mantha. Limbani mtima ndipo muona mmene Yehova atipulumutsire.’ Apa Mose anasonyeza kuti ankakhulupirira kwambiri Yehova.
Ndiyeno Yehova anauza Aisiraeli kuti anyamuke. Usiku umenewo, Yehova anachititsa kuti mtambo uja ukhale pakati pa Aisiraeliwo ndi Aiguputo. Zimenezi zinachititsa kuti kumbali ya Aiguputo kukhale mdima, pamene kumbali ya Aisiraeli kunkawala.
Yehova anauza Mose kuti atambasule dzanja lake n’kuloza panyanja. Ndiyeno Yehova anachititsa mphepo yamphamvu kuwomba panyanjapo usiku wonse. Kenako nyanjayo inagawikana ndipo madzi anaima ngati makoma m’mbali zonse. Aisiraeli anawoloka pouma kupita kutsidya la nyanjayo.
Asilikali a Farao analowa pakati pa makoma amadziwo potsatira Aisiraeli. Zitatero Yehova anachititsa kuti asilikaliwo asokonezeke. Mateyala a magaleta awo anayamba kuguluka. Ataona zimenezi asilikaliwo anafuula kuti: ‘Tiyeni tithawe! Yehova akuwamenyera nkhondo.’
Kenako Yehova anauza Mose kuti: ‘Tambasula dzanja lako ndi kuloza panyanja.’ Nthawi yomweyo madzi aja anabwerera m’malo mwake n’kumiza asilikali onse a Aiguputo. Farao ndi asilikali ake anafera pomwepo. Palibe ngakhale mmodzi amene anapulumuka.
Aisiraeliwo ataona kuti apulumuka anatamanda Mulungu poimba kuti: “Ndiimbira Yehova, chifukwa walemekezeka kwambiri. Mahatchi ndi okwera pamahatchiwo wawaponyera mʼnyanja.” Poimba nyimboyi, azimayi ankavina ndipo ena ankaimba maseche. Aliyense anasangalala kwambiri chifukwa tsopano sanalinso akapolo.
“Tikhale olimba mtima ndithu ndipo tinene kuti: ‘Yehova ndi amene amandithandiza. Sindidzaopa. Munthu angandichite chiyani?’”—Aheberi 13:6
-
-
Analonjeza Kuti Azimvera YehovaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 23
Analonjeza Kuti Azimvera Yehova
Patadutsa miyezi iwiri chichokereni ku Iguputo, Aisiraeli anafika paphiri la Sinai ndipo anamanga misasa. Yehova anauza Mose kuti akwere m’phirimo. Kumeneko anamuuza kuti: ‘Ndapulumutsa Aisiraeli. Ngati angandimvere komanso kusunga malamulo anga, adzakhala anthu anga apadera.’ Mose anatsika m’phirimo n’kukauza Aisiraeli zimene Yehova ananenazi. Kodi iwo anatani atamva zimenezi? Anayankha kuti: ‘Tidzachita chilichonse chimene Yehova wanena.’
Mose anapitanso kuphiri kuja. Ndiyeno Yehova anamuuza kuti: ‘Ndilankhula nanu pakadutsa masiku atatu. Uchenjeze anthu kuti asakwere phirili.’ Mose anatsika n’kukauza Aisiraeli kuti akonzekere kumva zimene Yehova adzawauze.
Patadutsa masiku atatu, kunayamba kuchita mphezi ndi mabingu ndipo paphiri lonselo panali mtambo wakuda. Kunamvekanso kulira kwa mphamvu kwa lipenga. Ndiyeno paphiripo panali moto kusonyeza kuti Yehova wabwera paphiripo. Aisiraeli anachita mantha kwambiri moti anayamba kunjenjemera. Phiri lonselo linkafuka utsi komanso linkagwedezeka kwambiri. Nalonso phokoso la lipenga lija linkawonjezereka. Ndiyeno Mulungu anati: ‘Ine ndine Yehova. Musamalambire milungu ina.’
Mose anakweranso m’phiri muja ndipo Yehova anamupatsa malamulo oti anthuwo azitsatira pomulambira komanso pochita zinthu zatsiku ndi tsiku. Mose analemba malamulowo n’kukawawerengera Aisiraeli. Iwo analonjeza kuti: ‘Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.’ Aisiraeliwo analonjeza kuti azimvera Mulungu. Koma kodi anachitadi zimenezi?
“Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, moyo wanu wonse ndi maganizo anu onse.”—Mateyu 22:37
-
-
Aisiraeli Sanachite Zimene AnalonjezaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 24
Aisiraeli Sanachite Zimene Analonjeza
Yehova anauza Mose kuti: ‘Bwera kuphiri kuno. Ndilemba malamulo anga pamiyala n’kukupatsa.’ Mose anapita kuphiriko ndipo anakhalako masiku 40. Ali komweko, Yehova analemba Malamulo 10 pamiyala iwiri n’kumupatsa.
Patapita nthawi, Aisiraeli anaganiza kuti Mose wawathawa. Choncho anauza Aroni kuti: ‘Tikufuna mtsogoleri wina. Tipangire mulungu.’ Aroni anawauza kuti: ‘Ndipatseni golide wanu.’ Ndiyeno anasungunula golideyo n’kupanga fano la mwana wa ng’ombe. Zitatero, Aisiraeliwo anati: ‘Uyu ndi Mulungu amene anatitulutsa m’dziko la Iguputo.’ Iwo anayamba kulambira fano la mwana wa ng’ombelo ndipo anachita mwambo wokondwerera fanolo. Kodi ukuganiza kuti zimenezi zinali zabwino? Ayi, chifukwa anthuwo anali atalonjeza kuti azilambira Yehova yekha. Koma zimene anachitazi zinali zosemphana ndi zimene analonjeza.
Yehova anaona zimene zinkachitikazi ndipo anauza Mose kuti: ‘Pita ukaone zimene anthu aja akuchita. Asiya kundimvera ndipo akulambira mulungu wabodza.’ Mose anatsika m’phirimo atanyamula miyala iwiri ija.
Atayandikira msasa uja anamva anthu akuimba. Kenako anawaona akuvina komanso kugwadira mwana wa ng’ombe uja. Mose anakwiya kwambiri. Anaponya pansi miyala iwiri ija moti inasweka. Nthawi yomweyo anawotcha fanolo n’kuliperapera. Kenako anafunsa Aroni kuti: ‘Kodi anthuwa akuchitira chiyani kuti uwamvere n’kuchita zinthu zoipa chonchi?’ Aroni anayankha kuti: ‘Pepani musandikwiyire. Mukudziwa bwino mmene anthuwa alili. Iwo amafuna mulungu ndiye ndinangotenga golide n’kumuponya pamoto ndipo panatuluka mwana wang’ombeyu.’ Komatu Aroni sankayenera kuchita zimenezi. Mose anapitanso kuphiri kuja n’kukapempha Yehova kuti akhululukire anthuwo.
Yehova anakhululukira anthu onse amene analapa n’kuyambiranso kumumvera. Kodi ukuona chifukwa chake zinali zofunika kuti Aisiraeli azimvera zonse zimene Mose ankawauza?
“Ukalonjeza kwa Mulungu usamachedwe kukwaniritsa lonjezo lako, chifukwa Mulungu sasangalala ndi anthu opusa. Uzikwaniritsa zinthu zimene walonjeza.”—Mlaliki 5:4
-
-
Chihema CholambiriramoZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 25
Chihema Cholambiriramo
Mose ali kuphiri la Sinai, Yehova anamuuza kuti akonze tenti yapadera yolambiriramo ndipo ankaitchula kuti chihema. Iwo anachikonza m’njira yoti azitha kuchinyamula kulikonse kumene akupita.
Yehova anauza Mose kuti: ‘Uza anthu kuti akupatse zinthu zimene angakwanitse kuti upangire chihema.’ Aisiraeli anapereka golide, siliva, kopa, miyala yamtengo wapatali komanso zodzikongoletsera. Anaperekanso ubweya wa nkhosa, nsalu, zikopa zanyama komanso zinthu zina zambiri. Anthuwo anapereka zinthu zambiri mpaka Mose anachita kuwauza kuti: ‘Basi zakwana. Musabweretsenso zina.’
Amuna ndi akazi ambiri aluso anagwira nawo ntchito yomanga chihemachi. Yehova anawapatsa nzeru zowathandiza pogwira ntchitoyi. Ena ankapanga ulusi, kuwomba nsalu komanso kuzikongoletsa. Panalinso ena amene ankapanga zinthu pogwiritsa ntchito miyala, golide kapena mitengo.
Anthuwo anapanga chihema potsatira malangizo amene Yehova anawapatsa. Anapanga katani yokongola imene inagawa Malo Oyera ndi Malo Oyera Koposa. M’Malo Oyera Koposa munali bokosi lotchedwa likasa la pangano. Bokosili linapangidwa ndi golide komanso matabwa a mtengo wa mthethe. M’Malo Oyera munali choikapo nyali chagolide, tebulo ndi guwa lansembe zofukiza. Ndipo pabwalo la chihema panali beseni lakopa ndi guwa lalikulu loperekera nsembe zopsereza. Likasa la pangano linkakumbutsa Aisiraeli kuti analonjeza zoti azimvera Yehova. Kodi ukudziwa kuti pangano n’chiyani? Ndi lonjezo lapadera limene anthu amachita.
Yehova anasankha Aroni ndi ana ake aamuna kuti azigwira ntchito kuchihema n’kumapereka nsembe. Ankayenera kusamalira chihemacho komanso kupereka nsembe kwa Yehova. Aroni yekha, yemwe anali mkulu wa ansembe ndi amene ankaloledwa kulowa m’Malo Oyera Koposa. Iye ankachita zimenezi kamodzi chaka chilichonse pokapereka nsembe ya machimo ake, a banja lake komanso a Aisiraeli onse.
Aisiraeli anamaliza kupanga chihemachi patangotha chaka chimodzi kuchokera pamene anatuluka m’dziko la Iguputo. Apa tsopano anali ndi malo olambirira Yehova.
Ulemerero wa Yehova unadzaza m’chihemacho ndipo mtambo unkakhala pamwamba pake. Mtambowo ukakhala pamwamba pa chihema, Aisiraeli ankakhalabe pamalo omwewo. Koma ukachoka, ankadziwa kuti nthawi yoti anyamuke yakwana. Choncho ankaphwasula chihema chija n’kumatsatira mtambowo ndipo ankakachimanga pamalo ena.
“Kenako ndinamva mawu ofuula kuchokera kumpando wachifumu akuti: ‘Taonani! Chihema cha Mulungu chili pakati pa anthu ndipo iye azidzakhala nawo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulunguyo adzakhala nawo.’”—Chivumbulutso 21:3
-
-
Anthu 12 Anapita Kukaona Dziko la KananiZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 26
Anthu 12 Anapita Kukafufuza Dziko la Kanani
Aisiraeli atachoka paphiri la Sinai anadutsa m’chipululu cha Parana n’kukafika pamalo otchedwa Kadesi. Ali pamalowa, Yehova anauza Mose kuti: ‘Sankha amuna 12 kuchokera mu fuko lililonse kuti apite kukaona dziko la Kanani limene ndikufuna kulipereka kwa Aisiraeli.’ Ndiyeno Mose anasankha amuna 12 n’kuwauza kuti: ‘Pitani ku Kanani mukaone ngati dzikolo ndi labwino kulimamo mbewu. Mukaonenso ngati anthu ake ali amphamvu kapena ofooka komanso ngati amakhala m’matenti kapena m’mizinda.’ Zitatero, anthuwo anauyamba ulendo wopita ku Kanani ndipo pa gululi panali Yoswa ndi Kalebe.
Patatha masiku 40, anthuwa anabwerera ndipo anatenga zipatso za nkhuyu, makangaza ndi mphesa. Iwo anati: ‘Dziko lake ndi labwino kwambiri koma anthu ake ndi amphamvu ndipo amakhala m’mizinda ya mipanda italiitali.’ Ndiyeno Kalebe anati: ‘Komabe tingathe kuwagonjetsa anthuwo. Tiyeni tipite pompano.’ Kodi ukudziwa chifukwa chake Kalebe ananena zimenezi? Chifukwa chakuti iye ndi Yoswa ankakhulupirira kwambiri Yehova. Koma anthu ena 10 aja anati: ‘Ayi tisapite. Anthu ake ndi akuluakulu komanso amphamvu moti ife timangooneka ngati tiziwala.’
Aisiraeli atamva zimenezi anakhumudwa kwambiri. Anayamba kudandaula kuti: ‘Tiyeni tisankhe mtsogoleri wina ndipo tibwerere ku Iguputo. Kodi pali chifukwa choti tipitire m’dziko limeneli n’kukaphedwa?’ Koma Yoswa ndi Kalebe anati: ‘Musapandukire Yehova ndipo musachite mantha. Yehova atiteteza.’ Komabe Aisiraeliwo sanamvere, moti mpaka ankafuna kupha Yoswa ndi Kalebe.
Kodi Yehova anatani? Iye anauza Mose kuti: ‘Aisiraeli ndawachitira zinthu zambirimbiri koma sakundimverabe. Chifukwa cha zimenezi, akhala m’chipululumu kwa zaka 40 ndipo onse afera momwemu. Anthu amene akalowe m’dziko limene ndalonjezali ndi ana awo okha limodzi ndi Yoswa komanso Kalebe.’
“N’chifukwa chiyani mukuchita mantha chonchi, anthu achikhulupiriro chochepa inu?”—Mateyu 8:26
-
-
Aisiraeli Ena Anaukira YehovaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 27
Aisiraeli Ena Anaukira Yehova
Nthawi ina Aisiraeli ali m’chipululu, Kora, Datani, Abiramu ndi anthu ena okwana 250 anaukira Mose. Iwo anati: ‘Tatopa nawe tsopano! N’chifukwa chiyani ukufuna uzitilamulira ndipo wasankha Aroni kuti akhale mkulu wa ansembe? Yehova ali ndi tonsefe, osati iweyo ndi Aroni basi.’ Zimenezi sizinamusangalatse Yehova chifukwa ankaona kuti anthuwo akutsutsana ndi iyeyo.
Mose anauza Kora ndi anthu amene anali kumbali ya Korayo kuti: ‘Mawa mubwere kuchihema ndipo mudzatenge zofukizira ndipo mʼzofukizirazo mudzaikemo moto ndi zinthu zonunkhira zoti mukapereke nsembe. Yehova adzationetsa munthu amene wamusankha.’
Tsiku lotsatira, Kora ndi anthu 250 aja anapitadi kukakumana ndi Mose kuchihema. Kumeneko iwo anapereka nsembe ngakhale kuti sanali ansembe. Yehova anauza Mose ndi Aroni kuti: ‘Chokani musayandikane ndi Kora ndi anzakewo.’
Ngakhale kuti Kora anapita kukakumana ndi Mose kuchihema, Datani, Abiramu ndi mabanja awo anakana kupitako. Yehova anauza Aisiraeli kuti asayandikire matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Nthawi yomweyo Aisiraeli anapita kutali ndi matentiwo. Datani, Abiramu ndi mabanja awo anaima panja pa matenti awo. Ndiye nthawi yomweyo nthaka inang’ambika n’kuwameza. Nakonso kuchihema kuja, moto wochokera kwa Yehova unapsereza Kora ndi anzake 250 aja.
Zitatero Yehova anauza Mose kuti: ‘Tenga ndodo ya mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ulembepo dzina la mtsogoleriyo. Koma pandodo ya fuko la Levi, ulembepo dzina la Aroni. Ndodozi uziike m’chihema ndipo ndodo ya munthu amene ndasankha, idzachita maluwa.’
Tsiku lotsatira Mose anatenga ndodo zonse n’kuwaonetsa atsogoleri aja. Ndodo ya Aroni inali itachita maluwa n’kubereka zipatso zakupsa za amondi. Zimenezi zinatsimikizira kuti Yehova anali atasankha Aroni kuti akhale mkulu wa ansembe.
“Muzimvera amene akukutsogolerani ndipo muziwagonjera.”—Aheberi 13:17
-