Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w03 3/15 tsamba 31
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
  • Nsanja ya Olonda—2003
  • Nkhani Yofanana
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuchita Chikumbutso cha Mgonero wa Ambuye?
    Nsanja ya Olonda—2003
  • “Muzichita Zimenezi Pondikumbukira”
    Nsanja ya Olonda—2013
  • N’chifukwa Chiyani Timachita Mwambo Wokumbukira Imfa ya Yesu?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Mwambo wa Chikumbutso Umasonyeza Makhalidwe a Mfumu Yakumwamba
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2003
w03 3/15 tsamba 31

Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Kodi pangachitidwe chinachake ngati Mkristu wodzozedwa yemwe akudwala sangathe kupezekapo pamene mpingo ukuchita mwambo wa Mgonero wa Ambuye?

Inde. Chinachake chingachitidwe ndipo chiyenera kuchitidwa posonyeza kuganizira Mkristu wodzozedwa yemwe akudwala ndipo mwina sachoka pamphasa, ndiyeno chifukwa cha zimenezi sangathe kupezekapo pamene mpingo ukuchita Chikumbutso cha imfa ya Kristu. Zikatere, bungwe la akulu lingakonze kuti mkulu kapena mwamuna wina wachikristu wokhwima mwauzimu atenge mkate ndi vinyo, zizindikiro za pa Chikumbutso, kupititsa kwa wokhulupirira mnzawoyo usiku womwewo umene mwambowo wachitika, ndipo akafikitse dzuwa lisanatuluke.

Mkulu kapena mbale amene wapita kwa Mkristu wodzozedwayo angapereke ndemanga zachidule ndi kuŵerenga malemba oyenerera, koma zimenezi zingadalire mmene alili. Angatsanzire chitsanzo cha Yesu pamene anayambitsa Mgonero wa Ambuye. Mwachitsanzo, akhoza kuŵerenga Mateyu 26:26 n’kupemphera ndiyeno n’kupereka mkate wopanda chotupitsawo. Kenako, mbale amene wabweretsa zizindikiroyo angaŵerenge Mateyu chaputala 26, vesi 27 ndi 28, n’kupempheranso ndiyeno n’kupereka vinyo. Angafotokoze mwachidule zimene chizindikiro chilichonse chikuimira, ndipo ayenera kumaliza ndi pemphero.

N’zoona kuti munthu ayenera kuyesetsa mmene angathere kuti apezekepo pamene mpingo ukuchita mwambo wa Mgonero wa Ambuye. Koma kodi n’chiyani chimene Mkristu wodzozedwa amene akudwala kwambiri, ali kuchipatala, kapena ali ndi vuto lina lake angachite ngati kutakhala kovutitsitsa kuti achite Chikumbutso dzuŵa litaloŵa pa Nisani 14? Wodzozedwa woteroyo angatsatire zimene zinkachitika m’Chilamulo cha Mose ndipo angachite mwambowo payekha patapita masiku 30.​—Numeri 9:9-14.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena