Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • jl phunziro 16
  • Kodi Atumiki Othandiza Ali Ndi Udindo Wotani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Atumiki Othandiza Ali Ndi Udindo Wotani?
  • Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
  • Nkhani Yofanana
  • Atumiki Othandiza Amagwira Ntchito Yofunika Kwambiri
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Kusunga Mgwirizano—Pakati pa Akulu ndi Atumiki Otumikira
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Atumiki Otumikira Amachita Ntchito Yofunika
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Akulu—Phunzitsani Ena Kusenza Maudindo
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
jl phunziro 16

PHUNZIRO 16

Kodi Atumiki Othandiza Ali Ndi Udindo Wotani?

Mtumiki wothandiza akuthandizira kugawa mabuku

Myanmar

Mtumiki wothandiza akuthandizira kugawa mabuku

Pamisonkhano

Mtumiki wothandiza akuthandizira kugawa mabuku

Kagulu ka Utumiki Wakumunda

Mtumiki wothandiza akugwira nawo ntchito yokonzanso zinthu pa Nyumba ya Ufumu

Kukonza pa Nyumba ya Ufumu

Baibulo limatchula magulu awiri a amuna achikhristu amene amakhala ndi maudindo mumpingo. Gulu loyamba ndi la “oyang’anira” ndipo lachiwiri ndi la “atumiki othandiza.” (Afilipi 1:1) Kawirikawiri mumpingo uliwonse mumakhala abale angapo amene ndi akulu komanso atumiki othandiza. Kodi atumiki othandiza amagwira ntchito zotani mumpingo?

Amathandiza bungwe la akulu. Atumiki othandiza, achinyamata ndi achikulire omwe, ndi amuna omwe ali paubwenzi wabwino ndi Yehova. Iwo amakhala odalirika komanso amachita zinthu mosamala. Atumiki othandiza amagwira ntchito zofunika zosiyanasiyana zomwe zimayenera kuchitika nthawi zonse. Zimenezi zimathandiza akulu kuti akwaniritse udindo wawo wophunzitsa komanso kuweta nkhosa za Mulungu.

Amagwira ntchito zosiyanasiyana pampingo. Atumiki othandiza amapatsidwa ntchito zosiyanasiyana, monga kulandira anthu amene akufika kumisonkhano, kusamalira zokuzira mawu, kusamalira mabuku. Komanso amasamalira ndalama za mpingo ndiponso amapatsa Akhristu anzawo dera loti azikalalikira. Iwo amathandizanso pa ntchito yokonza zinthu pa Nyumba ya Ufumu. Nthawi zina angapemphedwe ndi akulu kuti athandize okalamba. Atumiki othandiza amakhala ofunitsitsa kugwira ntchito iliyonse imene apatsidwa, ndipo zimenezi zimachititsa kuti onse mumpingo aziwalemekeza.​—1 Timoteyo 3:13.

Monga amuna achikhristu, iwo amapereka chitsanzo chabwino kwa ena. Atumiki othandiza amasankhidwa chifukwa cha makhalidwe awo achikhristu. Iwo amalimbitsa chikhulupiriro chathu akamakamba nkhani pamisonkhano. Komanso akamasonyeza chitsanzo chabwino pa ntchito yolalikira, amatithandiza kuti ifenso tikhale akhama. Popeza kuti iwo amamvera bungwe la akulu, zimenezi zimathandiza kuti onse azisangalala komanso kugwirizana. (Aefeso 4:16) Pakapita nthawi, iwonso angayenerere kukhala akulu.

  • Kodi atumiki othandiza ndi anthu otani?

  • Kodi atumiki amathandiza bwanji kuti mpingo uziyenda bwino?

DZIWANI ZAMBIRI

Nthawi iliyonse mukapita ku Nyumba ya Ufumu, yesetsani kudziwana ndi mkulu kapena mtumiki wothandiza mmodzi mpaka mutadziwana ndi onse limodzi ndi mabanja awo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena