Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Uthenga Wopita kwa Makolo
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Uthenga Wopita kwa Makolo

      Kodi mphatso yabwino kwambiri imene mungapatse ana anu ndi iti? Ana amafuna zinthu zambiri. Mwachitsanzo, iwo amafuna kuti muziwakonda, kuwauza zoyenera kuchita komanso kuwateteza. Komabe, mphatso yamtengo wapatali kwambiri imene mungapatse ana anuwo ndi kuwathandiza kuti am’dziwe Yehova ndi choonadi chopezeka m’Mawu ake, Baibulo. (Yohane 17:3) Zimenezi zingathandize anawo kuti azikonda Yehova ndi kum’tumikira ndi mtima wonse, kuyambira ali aang’ono.—Mateyu 21:16.

      Makolo ambiri akuona kuti ana aang’ono amaphunzira mofulumira ngati akuwaphunzitsa pang’onopang’ono ndi kuwauza zinthu zina zoti azichita. Choncho ndife osangalala kutulutsa kabuku kano kakuti Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo. Mutu uliwonse anaupanga m’njira yakuti ukhale wosavuta kuuphunzira. Kabuku kano talembera ana osapitirira zaka zitatu. Taikamo zithunzi ndi mawu ofotokozera zithunzizo komanso zoti ana azichita. Kabukuka si koti anawo aziseweretsa ayi, koma n’koti inuyo makolo muziwawerengera. Zimenezi zidzathandiza kuti muzikhala ndi nthawi yolankhulana ndi anawo.

      Tikukhulupirira kuti kabukuka kakuthandizani kwambiri pamene mukuphunzitsa ana anu choonadi cha m’Baibulo ‘kuyambira ali akhanda.’—2 Timoteyo 3:14, 15.

      Ndife abale anu,

      Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova

  • Phunziro 1
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 1

      Chivumbulutso 4:11

      Kodi ndani analenga dziko lapansili?

      Kodi ndani analenga nyanja?

      Kodi ndani analenga iweyo ndi ine?

      Kodi ndani analenga gulugufe wa mapiko okongola chonchi?

      Yehova Mulungu ndi amene analenga zinthu zonse.

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      Chivumbulutso 4:11

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Nyenyezi Mitambo Dzuwa

      Boti Dziko Nyumba

      Nyanja Gulugufe

      Mufunseni mwana wanu kuti:

      Kodi dzina la Mulungu ndani?

      Kodi Yehova amakhala kuti?

      Kodi Yehova analenga zinthu ziti?

  • Phunziro 2
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 2

      Genesis 7:7-10; 8:15-17

      Waziona nyama zimene zili pafupi ndi chingalawa cha Nowa?

      Kodi ndi nyama ziti zimene zimalira kuti moo? Nanga ndi ziti zimene zimauwa?

      Chingalawa cha Nowa chinapulumutsa nyama zonse, zazifupi ndi zazitali zomwe.

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      Genesis 7:7-10; 8:15-17

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Chimbalangondo Galu Njovu

      Kadyansonga Mkango Nyani

      Nkhumba Nkhosa

      Mbidzi Utawaleza

      Muuzeni mwanayo kuti ayerekezere mmene nyama izi zimalirira:

      Galu Mbuzi Tambala

      Nkhumba Ng’ombe

  • Phunziro 3
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 3

      1 Petulo 3:8

      Davide wamva zoti mnzake akudwala.

      Choncho akunena kuti: “Ndadziwa chochita.

      Ndimulembera kalata yomulimbikitsa, ndipo kenako ndikam’patsa.”

      Uzisonyeza ena chifundo, ndipo nonse mudzakhala osangalala.

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      1 Petulo 3:8

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Nyumba Tebulo Davide

      Dzuwa Mbalame Mtengo

      Mufunseni mwana wanu kuti:

      Kodi ukudziwa aliyense amene akudwala?

      Kodi tingamuthandize bwanji kuti achire?

  • Phunziro 4
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 4

      Machitidwe 14:17

      Tsiku lina kunja kunkagwa mvula.

      Choncho Tomoko anadandaula kuti:

      “Ndikulephera kutuluka.

      N’chifukwa chiyani mvulayi sikusiya?”

      Koma kenako,

      mvula ija inasiya.

      Ndipo dzuwa linawala.

      Tomoko anasangalala kwambiri.

      Ndiyeno anathamanga kupita panja ndipo anadabwa kwambiri ndi zimene anaona.

      Tomoko ananena kuti, “Sindimadziwa kuti mvula yochokera kwa Mulungu, imakulitsa maluwa.”

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      Machitidwe 14:17

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Windo Mbalame Tomoko

      Mtengo Maluwa

      Pezani zinthu zobisika.

      Kachilombo Ndege

      Mufunseni mwana wanu kuti:

      N’chifukwa chiyani Yehova analenga mvula?

  • Phunziro 5
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 5

      1 Atesalonika 5:18

      Mnzako akakupatsa mphatso kapena kukuchitira zabwino umanyadira ndipo umasekerera.

      Komabe nthawi zonse uzikumbukira kunena kuti “Zikomo.”

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      1 Atesalonika 5:18

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Mphatso Mnyamata

      Chitseko Chakudya

      Pezani zinthu zobisika.

      Apozi Telefoni

      Mufunseni mwana wanu kuti:

      N’chifukwa chiyani ndi bwino kunena kuti “Zikomo”?

  • Phunziro 6
    Zimene Ndikuphunzira M’Baibulo
    • Phunziro 6

      Salimo 139:14

      Tayang’ana zala zako za m’manjazo ndipo ugwedeze zala zako za kumiyendo.

      Loza makutu ako, kenako uloze mphuno yako.

      Tayang’ana miyendo yakoyo. Miyendo imeneyi ndi yomwe imakuthandiza kuti uzitha kuthamanga, kudumpha, kupanga masewera ozungulira ndi masewera ena osiyanasiyana.

      Yang’ana pagalasi. Kodi ukuona chiyani?

      Zonse zimene Yehova anapanga n’zabwino kwambiri.

      ZOTI MUCHITE

      Mwana wanuyo muwerengereni:

      Salimo 139:14

      Muuzeni mwanayo kuti aloze:

      Zala zake zam’manja Zala zake zakumiyendo Mphuno yake

      Makutu ake Pakamwa pake

      Pezani zinthu zobisika.

      Nkhanu Mphaka

      Mufunseni mwana wanu kuti:

      Kodi ndani analenga iweyo ndi ine?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena