Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 10/09 tsamba 8-9
  • Mfundo 7: Muzitsatira Malangizo Odalirika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo 7: Muzitsatira Malangizo Odalirika
  • Galamukani!—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Pali Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja?
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Kodi Kutha kwa Banja Kumakhudza Bwanji Ana?
    Galamukani!—2009
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Banja?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Ngati Ukwati Ukufuna Kusweka
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
Onani Zambiri
Galamukani!—2009
g 10/09 tsamba 8-9

Mfundo 7: Muzitsatira Malangizo Odalirika

Mungachite bwanji? Banja lili ngati nyumba. Kuti nyumba ikhale yolimba imafunika kumangidwa pamaziko abwino. Nalonso banja kuti likhale lolimba, mwamuna ndi mkazi wake amafunika kutsatira malangizo odalirika.

Kufunika kwake. Malangizo a m’banja akupezeka paliponse monga m’mabuku, m’magazini, ndiponso m’mapulogalamu a pa TV. Alangizi ena amauza anthu amene ali ndi mavuto a m’banja kuti asathetse ukwati wawo pamene ena amawauza kuti angothetsa ukwatiwo. Ndiponso akatswiri amasinthasintha maganizo awo. Mwachitsanzo m’chaka cha 1994, dokotala wina wotchuka, yemwe ndi katswiri pankhani za achinyamata, analemba kuti atangoyamba ntchito yake, ankaona kuti “ana amasangalalako banja likatha n’kumakhala ndi bambo kapena mayi okha kuyerekeza ndi kukhala ndi makolo onse awiri amene sagwirizana.” Iye anati: “Ndinkaganiza kuti kuthetsa banja ndi kwabwino kuyerekeza ndi kukhalabe m’banja lamavuto.” Koma patapita zaka ziwiri dokotalayu anasintha maganizo ake ndipo ananena kuti: “Ukwati ukatha ana amavutika kwambiri.”

Maganizo a anthu amatha kusintha, koma malangizo abwino kwambiri ayenera kugwirizana ndi mfundo zopezeka m’Mawu a Mulungu, Baibulo. Pamene mumawerenga nkhanizi mwina mwaona kuti mfundo ya m’Baibulo yalembedwa pamwamba, kuyambira tsamba 3 mpaka 8. Mfundo zimenezi zathandiza mabanja ambiri kuti aziyenda bwino. N’zoona kuti mabanja amenewa amakumananso ndi mavuto, komabe amayenda bwino chifukwa amatsatira malangizo odalirika a m’Baibulo. Malangizo a m’Baibulo ndi odalirika chifukwa Baibulo linalembedwa ndi Yehova Mulungu yemwenso anayambitsa banja.—2 Timoteyo 3:16, 17.

Yesani izi. Lembani penapake malemba amene ali pamwamba pa tsamba 3 mpaka 8. Mungawonjezerenso malemba ena amene akuthandizani. Asungeni kuti muziwagwiritsa ntchito.

Chitani izi. Yesetsani kutsatira mfundo za m’Baibulo m’banja lanu.

[Chithunzi pamasamba 8, 9]

Kuti nyumba ikhale yolimba imafunika kumangidwa pamaziko abwino. Maziko abwino a banja ndi malangizo odalirika a m’Baibulo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena