Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kusangalala Unansi Wabwino wa Apongozi
    Galamukani!—1990 | March 8
    • Kuzindikira Chomangira Chatsopano

      Baibulo limapereka chithunzi chabwino cha kakonzedwe kaukwati Wam’malemba. Pamene Mulungu analenga aŵiri oyambirira ndikuwaika pamodzi, iye anakhazikitsa lamulo lotsatirapo iri: “Mwamuna adzasiya atate wake ndi amake nadzaphatika kwa mkazi wake: ndipo adzakhala thupi limodzi” (Genesis 2:24) Chotero okwatirana chatsopanowo ayenera kuzindikira kuti iwo aloŵa m’chomangira chatsopano. Iwo tsopano ayenera kumamatirana monga banja loima palokha ngakhale ngati angakhale ndi apongozi ndi azilamu awo.

      Komabe, kusiya atate ndi amayi, sikumatanthauza kuti pamene ana akwatirana ayenera kunyalanyaza makolo awo ndikuti sakufunikiranso kuwalemekeza ndi kuwapatsa ulemu. “Usapeputse amako atakalamba,” ikulangiza tero Baibulo. (Miyambo 23:22) Komabe, mu ukwati, muli kusintha kwa m’maunansi. Malinga ngati chiŵalo chirichonse chabanja chikumbukira mfundoyi, okwatirana achichepere angapindule ndi zokumana nazo ndi nzeru za makolo.

  • Kusangalala Unansi Wabwino wa Apongozi
    Galamukani!—1990 | March 8
    • Pamenepa, kodi ndimotani mmene mwamuna angakhalire ndi mbali yokangalika m’kupanga mtendere m’banja lake? Mitsuharu akunena kuti kugwiritsira ntchito kwake malamulo a makhalidwe abwino a Baibulo kunathandiza banja lake. “Chomangira pakati pa amai ndi mwana wawo wamwamuna nchamphamvu kwanbiri ngakhale kuti mwanayo wakula kukhala mwamuna wachikulire,” iye akuvomereza tero, “chotero mwana ayenera kupanga kuyesayesa kwamphamvu ‘kusiya atate wake ndi amake ndi kukamamatira kwa mkazi wake.’” Iye anagwiritsira ntchito lamulo la makhalidwe abwino mwa kukambitsirana nkhani zokhudza kusamalira ndi kulangiza ana ndi mkazi wake yekha, ndipo sanayerekezere mkazi wake kwa amake ponena za ntchito panyumba. “Tsopano,” iye akupitiriza tero, “ife ndi makolo anga timalemekezana. Aliyense wa ife amadziŵa nthaŵi pamene kuloŵerera kudzakanidwa ndi pamene thandizo ndi kugwirizanika zidzayamikirika.”

      Kuwonjezera pa ‘kumamatira kwa mkazi wake,’ mwamuna ayenera kukhala mtetezi pakati pa amake ndi mkazi wake. (Genesis 2:24) Ayenera kukhala womvetsera wabwino ndi kuwalola kutsanulira zakukhosi kwawo. (Miyambo 20:5) Mwamuna wina wokwatira, amene waphunzira kusamalira mikhalidweyo mwaluso, choyamba amafuna kudziŵa m’mene mkazi wake akulingalira. Pamenepo, iye amalankhula kwa amake za nkhaniyo, pamaso pa mkazi wake. Mwakusenza thayo lake mwanjirayo monga wopanga mtendere, mwana wamwamunayo angathandizire kupanga maunansi osangalatsa m’banja pakati pa akazi aŵiri amene iye amakonda.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena