-
Pezani Chitonthozo kwa YehovaNsanja ya Olonda—1996 | November 1
-
-
6. (a) Kodi ndi lonjezo lotonthoza lotani limene Mulungu anapereka pamene anthu anagwera m’tchimo? (b) Kodi Lameke anapereka ulosi wotani wonena za chitonthozo?
6 Poweruza amene anasonkhezera munthu kupanduka, Yehova anasonyeza kuti ali ‘Mulungu wa chitonthozo.’ (Aroma 15:5) Iye anachita zimenezo mwa kulonjeza kutumiza “mbewu” imene potsirizira pake idzamasula mbadwa za Adamu ku ziyambukiro zatsoka za chipanduko cha Adamu. (Genesis 3:15) M’kupita kwa nthaŵi, Mulungu anaperekanso zizindikiro za chilanditso chimenechi. Mwachitsanzo, anauzira Lameke, mbadwa yapatali ya Adamu kupyolera mwa mwana wake Seti, kunenera za zimene mwana wa Lameke adzachita: “Yemweyu adzatonthoza mtima wathu pa ntchito zathu zovuta za manja athu, chifukwa cha nthaka imene anaitemberera Yehova.” (Genesis 5:29) Mogwirizana ndi lonjezo limeneli, mnyamatayo anatchedwa Nowa, dzina limene limadziŵika kutanthauza “Kupuma” kapena “Chitonthozo.”
-
-
Pezani Chitonthozo kwa YehovaNsanja ya Olonda—1996 | November 1
-
-
8 Yehova anafuna kuwononga dziko loipalo ndi chigumula cha dziko lonse, koma choyamba anauza Nowa kuti amange chingalawa chopulumutsiramo moyo. Chifukwa chake, fuko la anthu ndi mitundu ya nyama inapulumutsidwa. Nowa ndi banja lake ayenera kuti anapeza mpumulo chotani nanga Chigumulacho chitapita pamene anatuluka m’chingalawacho kuloŵa m’dziko loyeretsedwa! Nkotonthoza mtima chotani nanga kudziŵa kuti temberero pa nthaka linachotsedwa, zikumapangitsa ntchito yaulimi kukhala yopepuka kwambiri! Ndithudi, ulosi wa Lameke unakhaladi woona, ndipo Nowa anakwaniritsa tanthauzo la dzina lake. (Genesis 8:21) Monga mtumiki wokhulupirika wa Mulungu, Nowa anagwiritsiridwa ntchito kudzetsa ‘chitonthozo’ kwa anthu pamlingo winawake. Komabe, chisonkhezero choipa cha Satana ndi angelo ake auchiŵanda sichinathere pa Chigumula, ndipo anthu akupitiriza kubuula m’goli la uchimo, matenda, ndi imfa.
-