-
Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani Yodzikonda Wekha?Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
-
-
Baibulo limanenanso za lamulo lachiwiri kuti: “Uzikonda mnzako mmene umadzikondera wekha.”—Maliko 12:31; Levitiko 19:18.
Ngakhale kuti Baibulo silinapereke lamulo lachindunji loti munthu azidzikonda yekha, koma mawu akuti “uzikonda mnzako mmene umadzikondera wekha,” akusonyeza kuti sikolakwika ngati munthu atamadzikonda yekha komanso kudzisungira ulemu mosapitirira malire.
-
-
Kodi “Kukonda Adani Anu” Kumatanthauza Chiyani”?Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
-
-
Maganizo olakwika: Chilamulo cha Mulungu chinkalola Aisiraeli kuti azidana ndi adani awo.
Zoona zake: M’chilamulo munalibe lamulo limeneli. Koma chinkalimbikitsa Aisiraeli kuti azikonda anzawo. (Levitiko 19:18) Ngakhale kuti mawu akuti “mnzako” anganene za munthu wina aliyense, Ayuda ena ankaona kuti mawuwa ankanena za Ayuda anzawo basi, ndipo ankakhulupirira kuti anthu amene sanali Ayuda anali adani awo ndipo ankayenera kudana nawo. (Mateyu 5:43, 44) Yesu anawongolera maganizo olakwikawo powauza fanizo la Msamariya wachifundo.—Luka 10:29-37.
-