-
“Israyeli wa Mulungu” ndi “Khamu Lalikulu”Nsanja ya Olonda—1995 | July 1
-
-
8 Israyeli, pamene anali wokhulupirika, anavomereza ulamuliro wa Yehova ndi kumlandira kukhala Mfumu yawo. (Yesaya 33:22) Motero, iwo anali ufumu. Koma, monga momwe kunasonyezedwera pambuyo pake, lonjezo lonena za “ufumu” likatanthauzadi zochuluka kuposa zimenezo. Ndiponso, pamene anamvera Chilamulo cha Yehova, anali oyera, olekana ndi mitundu yowazinga. Anali mtundu wopatulika. (Deuteronomo 7:5, 6) Kodi iwo anali ufumu wa ansembe? Chabwino, mu Israyeli fuko la Levi linapatulidwa kaamba ka utumiki wa pakachisi, ndipo mu fukolo munali kagulu ka ansembe Achilevi. Pamene Chilamulo cha Mose chinakhazikitsidwa, amuna Achilevi anatengedwa mosinthanitsana ndi mwana wachisamba aliyense wa m’banja losakhala la Alevi.a (Eksodo 22:29; Numeri 3:11-16, 40-51) Motero, banja lililonse mu Israyeli linali ndi oliimira, titero kunena kwake, mu utumiki wa pakachisi. Mwanjira imeneyo mtunduwo unakhala wa ansembe. Chikhalirechobe, uwo unaimira Yehova pamaso pa mitundu ina. Mlendo aliyense amene anafuna kulambira Mulungu woona anafunikira kuchita motero mogwirizana ndi Israyeli.—2 Mbiri 6:32, 33; Yesaya 60:10.
-
-
“Israyeli wa Mulungu” ndi “Khamu Lalikulu”Nsanja ya Olonda—1995 | July 1
-
-
a Pamene unsembe wa Israyeli unakhazikitsidwa, ana aamuna achisamba a mafuko a Israyeli osakhala a Alevi ndi amuna Achilevi anaŵerengedwa. Panali ana achisamba 273 owonjezereka kuposa amuna Achilevi. Motero, Yehova analamula kuti masekeli asanu pa munthu aliyense wa 273 amenewo aperekedwe monga dipo la kuchulukitsitsako.
-