-
Yehova Aŵerengeretu Bwino Mlandu WanuNsanja ya Olonda—1996 | September 15
-
-
“Mundikumbukire . . . Mulungu wanga, . . . Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.”—NEHEMIYA 13:22, 31.
-
-
Yehova Aŵerengeretu Bwino Mlandu WanuNsanja ya Olonda—1996 | September 15
-
-
2. (a) Kodi Nehemiya anadziŵerengera bwino motani mlandu wa iye mwini kwa Mulungu? (b) Kodi Nehemiya anamaliza buku la m’Baibulo la dzina lake ndi pempho lotani?
2 Mwamuna wina amene anadziŵerengera bwino mlandu wake kwa Mulungu anali Nehemiya, wopereka chikho wa Mfumu yachiperisiya Aritasasta (Longimanus). (Nehemiya 2:1) Nehemiya anakhala bwanamkubwa wa Ayuda ndipo anamanga malinga a Yerusalemu akumayang’anizana ndi adani ndi ngozi. Pokhala ndi changu cha kulambira koona, anachirikiza Chilamulo cha Mulungu ndi kusonyeza nkhaŵa kaamba ka oponderezedwa. (Nehemiya 5:14-19) Nehemiya analimbikitsa Alevi kudziyeretsa nthaŵi zonse, kulonda zipata, ndi kupatula tsiku la Sabata. Motero anatha kupemphera kuti: “Mundikumbukire ichinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa chifundo chanu chachikulu.” Moyenereranso, Nehemiya anamaliza buku lake louziridwa ndi Mulungu ndi pempho lakuti: “Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.”—Nehemiya 13:22, 31.
-