Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yehova Aŵerengeretu Bwino Mlandu Wanu
    Nsanja ya Olonda—1996 | September 15
    • “Mundikumbukire . . . Mulungu wanga, . . . Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.”​—NEHEMIYA 13:22, 31.

  • Yehova Aŵerengeretu Bwino Mlandu Wanu
    Nsanja ya Olonda—1996 | September 15
    • 2. (a) Kodi Nehemiya anadziŵerengera bwino motani mlandu wa iye mwini kwa Mulungu? (b) Kodi Nehemiya anamaliza buku la m’Baibulo la dzina lake ndi pempho lotani?

      2 Mwamuna wina amene anadziŵerengera bwino mlandu wake kwa Mulungu anali Nehemiya, wopereka chikho wa Mfumu yachiperisiya Aritasasta (Longimanus). (Nehemiya 2:1) Nehemiya anakhala bwanamkubwa wa Ayuda ndipo anamanga malinga a Yerusalemu akumayang’anizana ndi adani ndi ngozi. Pokhala ndi changu cha kulambira koona, anachirikiza Chilamulo cha Mulungu ndi kusonyeza nkhaŵa kaamba ka oponderezedwa. (Nehemiya 5:14-19) Nehemiya analimbikitsa Alevi kudziyeretsa nthaŵi zonse, kulonda zipata, ndi kupatula tsiku la Sabata. Motero anatha kupemphera kuti: “Mundikumbukire ichinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa chifundo chanu chachikulu.” Moyenereranso, Nehemiya anamaliza buku lake louziridwa ndi Mulungu ndi pempho lakuti: “Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.”​—Nehemiya 13:22, 31.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena