-
Mtendere—ZenizenizoNsanja ya Olonda—1989 | December 15
-
-
“[2] Ndipo kudzakhala masiku otsiriza, kuti phiri la nyumba ya Yehova lidzakhazikika pa nsonga ya mapiri, ndipo lidzakwezedwa pamwamba pa zitunda; mitundu yonse idzasonkhana kumeneko. [3] Ndipo anthu ambiri adzanka, nati, Tiyeni tikwere kunka ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo; ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zake, ndipo tidzayenda m’mayendedwe ake; chifukwa m’Ziyoni mudzatuluka chilamulo, ndi mawu a Yehova kuchokera m’Yerusalemu. [4] Iye adzaweruza pakati pa akunja, adzadzudzula mitundu yambiri ya anthu; ndipo iwo adzasula malupanga awo akhale zolimira, ndi nthungo zawo zikhale anangwape; mtundu sudzanyamula lupanga kumenyana ndi mtundu wina, ndipo sadzaphunziranso nkhondo.”
-
-
Mtendere—ZenizenizoNsanja ya Olonda—1989 | December 15
-
-
Kodi bwanji ponena za lerolino? Onani kuti Yesaya akuyamba uthenga wake ndi ndemanga yakuti: “Ndipo kudzakhala masiku otsiriza.” Matembenuzidwe ena amati: “M’masiku otsiriza.” (New International Version) Umboni umaperekedwa mokhazikika m’masamba a magazine ano kuchilikiza kuti takhala tikukhala m’masiku otsiriza a dziko liripoli chiyambire 1914. Chotero, kodi nchiyani chimene tiyenera kuyembekezera kuwona, mogwirizana ndi mavesi 3 ndi 4?
-
-
Mtendere—ZenizenizoNsanja ya Olonda—1989 | December 15
-
-
Mneneriyo akulongosola kuti “phiri la nyumba ya Yehova lidzakhazikika pa nsonga ya mapiri” ndipo “lidzakwezedwa pamwamba pa zitunda.” M’nthaŵi zakale, mapiri ena ndi zitunda zinatumikira monga malo a kulambira mafano ndi malo opatulika a milungu yonyenga. Pamene Mfumu Davide anabweretsa Likasa lopatulika ku hema woikidwa pa Phiri la Ziyoni (Yerusalemu), mamita 760 pamwamba pa malekezero a nyanja, iye mwachiwonekere ankachita mogwirizana ndi chitsogozo cha Mulungu. Pambuyo pake, pamene kachisi wamkulu wa Yehova anamangidwa pa Phiri la Moriya, liwu lakuti “Ziyoni” linafikira pa kuphatikiza malo a kachisi, chotero kachisi analinso pa malo okwezeka kuposa malo ozungulira achikunja. Yerusalemu weniweniyo ankatchedwanso “phiri lopatulika”; mwakutero, kulambira kwa Yehova kunakhalabe pa malo okwezeka.—Yesaya 8:18; 66:20.
Chotero lerolino, kulambira kwa Yehova Mulungu kwakhala kokwezeka mofanana ndi phiri lophiphiritsira. Kutchuka kwake nkofunikira kuti onse akuwone, popeza kwachita chinachake chimene palibe chipembedzo china chirichonse chimene chakhala chokhoza kuchichita. Kodi icho nchiyani? Iko kwagwirizanitsa alambiri onse a Yehova, amene mwachimwemwe asula malupanga awo kukhala zolimira ndipo sakuphunziranso nkhondo. Zoletsa zautundu ndi ufuko siziwalekanitsanso. Iwo amakhala monga anthu ogwirizana,paubale, ngakhale kuti ali omwazikana m’mitundu yonse ya dziko.—Salmo 33:12.
-