-
“Ali ndi Mtima Wanzeru” Koma Ndi WodzichepetsaYandikirani Yehova
-
-
3 Yehova ndi woyera. Choncho iye si wodzikuza chifukwa kudzikuza kumaipitsa munthu. (Maliko 7:20-22) Taonani zimene mneneri Yeremiya anauza Yehova. Iye anati: “Ndithu mudzandikumbukira ndi kundiweramira kuti mundithandize.”a (Maliro 3:20) Tangoganizani. Yehova Ambuye Wamkulu Koposa anali wofunitsitsa ‘kuwerama,’ kapena kuti kugwada kuti afanane msinkhu ndi Yeremiya, n’cholinga choti athandize munthu yemwe sanali wangwiroyu. (Salimo 113:7) Kunena zoona, Yehova ndi wodzichepetsa. Koma kodi Mulungu amasonyeza bwanji kuti ndi wodzichepetsa? Kodi kudzichepetsa n’kogwirizana bwanji ndi kukhala wanzeru? Nanga kudzichepetsa kwa Yehova kumatithandiza bwanji?
-
-
“Ali ndi Mtima Wanzeru” Koma Ndi WodzichepetsaYandikirani Yehova
-
-
a Anthu ena akale omwe ankakopera Baibulo otchedwa Asoferimu anasintha vesili kuti lizimveka ngati Yeremiya ndi amene akuwerama osati Yehova. Zikuoneka kuti iwo ankaganiza kuti n’zosayenera kunena kuti Mulungu angachite zinthu modzichepetsa chonchi kuti athandize munthu. Chifukwa cha zimenezi, Mabaibulo ambiri sanamasulire bwino mfundo yosangalatsa imene ili m’vesili. Komabe, Baibulo lina linamasulira molondola kuti Yeremiya anauza Mulungu kuti: “Kumbukirani, kumbukirani ndipo mundiweramire.”—The New English Bible.
-