-
“Kachisi” ndi “Kalonga” LerolinoNsanja ya Olonda—1999 | March 1
-
-
3. Kodi tsindwi lam’mwambalo ndi mitengo ya kanjedza yozokotedwa m’makoma a njira zoloŵera m’kachisi zikutiphunzitsanji?
3 Tayerekezerani kuti tikuyendera kachisi wa m’masomphenya ameneyu. Tikukwera masitepe asanu ndi aŵiri kupita kuchipata china chachikulu. Titaloŵa pakhomopo, tikuyang’ana m’mwamba ndi kudabwa. Tsindwi lake lili mamita oposa 30 m’mwamba! Zimenezo zikutikumbutsa kuti zofunika zoloŵera m’makonzedwe a Yehova a kulambira n’zapamwamba. Kuŵala koloŵera m’mazenera kukuunika mitengo yakanjedza yozokotedwa kumakoma, imene Malemba amagwiritsa ntchito kuimira chilungamo. (Salmo 92:12; Ezekieli 40:14, 16, 22) Malo opatulika ameneŵa ndi a anthu olungama m’makhalidwe ndi mwauzimu. Pogwirizana ndi zimenezo, ifenso tikhale olungama kuti Yehova avomereze kulambira kwathu.—Salmo 11:7.
-
-
“Kachisi” ndi “Kalonga” LerolinoNsanja ya Olonda—1999 | March 1
-
-
5. (a) Kodi masomphenya a Ezekieli ndi masomphenya a Yohane olembedwa pa Chivumbulutso 7:9-15 akufanana motani? (b) M’masomphenya a Ezekieli, kodi mafuko 12 amene akulambira kubwalo lakunja akuimira ayani?
5 Njirayo ikutulukira kubwalo lakunja, kumene anthu akulambira ndi kutamanda Yehova. Zimenezi zikutikumbutsa za masomphenya a mtumwi Yohane a “khamu lalikulu” lolambira Yehova “usana ndi usiku m’Kachisi mwake.” Mitengo yakanjedza ikusonyezedwa m’masomphenya aŵiriwo. M’masomphenya a Ezekieli, ikukometsera makoma a njira yoloŵera. M’masomphenya a Yohane, olambira ali ndi makhwata a kanjedza m’manja mwawo, kuimira chimwemwe chawo potamanda Yehova ndi pochingamira Yesu monga Mfumu. (Chivumbulutso 7:9-15) M’nkhani ya masomphenya a Ezekieli, mafuko 12 a Israyeli akuimira “nkhosa zina.” (Yohane 10:16; yerekezerani ndi Luka 22:28-30.) Kodi ndinu mmodzi wa awo amene akupeza chimwemwe potamanda Yehova mwa kulengeza Ufumu wake?
-